home >>stonecroft>> 
            >> mavesi 
            a m'baibulo >> phunziro 4 >> phunziro 5             
            
             
                       MULUNGU ALI NGATI CHIYANI? - Mavesi a m'Baibulo - Phunziro 5      
                        Mavesi a m'Baibulo 
            Kuwerenga Baibulo kwa Mlungu ndi Mlungu 
Yeremiya 29:13 
            13Ndipo mudzandifuna Ine, ndi kundipeza, pamene mundifuna ndi mtima 
            wanu wonse.
            Yohane 14: 21-23 
              21Iye wakukhala nao malamulo anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda 
              Ine; koma wondikonda Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo line 
              ndidzamkonda, ndipo ndidzadzionetsandekha kwa iye. 22Yudase, si 
              Isikariote, ananena ndi iye, Ambuye, cacitika ciani kuti muziti 
              mudzionetsa nokha kwa ife, koma si kwa dziko lapansi? 23Yesu anayankha 
              nati kwa iye, Ngati wina akonda Ine, adzasunga mau anga; ndipo Atate 
              wanga adzamkonda, ndipo tidzadza kwa iye, ndipo tidzayesa kwa iye 
              mokhalamo.  
            Aroma 5: 6-9 
              6Pakuti pamene tinali cikhalire ofok a, pa nyengo yace Kristu anawafera 
              osapembedza. 7Pakuti ndi cibvuto munthu adzafera wina wolungama; 
              pakuti kapena wina adzalimbika mtima kufera munthu wabwino. 8Koma 
              g Mulungu atsimikiza kwa ife cikonai cace ca mwini yekha m'menemo, 
              kuti pokhala ife cikhalire ocimwa, Kristu adatifera ife. 9Ndipo 
              tsono popeza inayesedwa olungama ndi mwazi wace, makamaka ndithu 
              tidzapulumuka mkwiyo wa Mulungu mwa Iyeyo. 
            1 Timoteo 2: 1-6 
              1Ndidandaulira tsono, poyambayamba, kuti acitike mapembedzo, mapemphero, 
              mapembedzero, mayamiko, cifukwa ca anthu onse; 2cifukwa ca mafumu 
              ndi onse akucita ulamuliro kuti m'moyo mwathu tikakhale odika mtima, 
              ndi acete m'kulemekeza Mulungu, ndi m'kulemekezeka monse. 3Pakuti 
              ici ncokoma ndi colandirika pamaso pa Mulungu Mpulumutsi wathu; 
              4amene afuna anthu onse apulumuke, nafike pozindikira coonadi. 5Pakuti 
              pali Mulungu mmodzi, ndi Mtetezi mmodzi pakati pa Mulungu ndi anthu, 
              ndiye munthu, Kristu Yesu, 6amene anadzipereka yekha ciombolom'malo 
              mwa onse; umboni m'nyengo zace;  
            Yakobo 4: 7-10 
              7Potero mverani Mulungu; koma kanizani mdierekezi, ndipo adzakuthawani 
              inu. 8Yandikirani kwa Mulungu, ndipo adzayandikira kwa inu, Sambani 
              m'manja, ocimwa inu; yeretsani mitima, a mitima iwiri inu. 9Khalani 
              osautsidwa, lirani, lirani misozi; kuseka kwanu kusanduke kulira, 
              ndi cimwemwe canu cisanduke cisoni. 10Dzicepetseni pamaso pa Ambuye, 
              ndipo adzakukwezani. 
            2 Petro 3: 9 
              9Ambuye sazengereza nalo lonjezano, monga ena aciyesa cizengerezo; 
              komatu aleza mtima kwa inu, wosafuna kuti ena aonongeke, koma kuti 
              onse afike kukulapa. 
            Ahebri 11: 6 
              6koma wopanda cikhulupiriro sikutheka kumkondweretsa; pakuti iye 
              wakudza kwa Mulungu ayenera kukhulupirira kuti alipo, ndi kuti ali 
              wobwezera mphotho iwo akumfuna iye.  
            Mateyu 11: 27-30 
              27Zinthu zonse zinaperekedwa kwa Ine ndi Atate wanga; ndipo palibe 
              munthu adziwa Mwana, koma Atate yekha; ndi palibe wina adziwa Atate, 
              koma M wana yekha, ndi iye amene Mwana afuna kumuululira. 28Idzani 
              kuno kwa Ine nonsenu akulema ndi akuthodwa, ndipo Ine ndidzakupumulitsani 
              inu. 29Senzani gori langa, ndipo phunzirani kwa Ine; cifukwa ndiri 
              wofatsa ndi wodzicepetsa mtima: ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo 
              yanu. 30Pakuti 1 gori langa liri lofewa, ndi katundu wanga ali wopepuka. 
                    Funso #1 
     Masalmo 46:10 
              10Khalani cete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu: Ndidzabuka 
              mwa amitundu, Ndidzabuka pa dziko lapansi. 
            Masalmo 145: 18-19 
              18Yehova ali pafupi ndi onse akuitanira kwa Iye, Onse akuitanira 
              kwa Iye m'coonadi. 
              19Adzacita cokhumba iwo akumuopa; Nadzamva kupfuula kwao, nadzawapulumutsa. 
            Yesaya 55: 3 
              3Cherani Lhutu lanu, mudze kwa Ine, imvani, mzimu wanu nudzakhala 
              ndi moyo; ndipo ndidzapangana nanu cipangano cosatha, ndico zifundo 
              zoona za Davide. 
            Ahebri 10:22 
              22tiyandikire ndi mtima woona, m'cikhulupiriro cokwanira, ndi mitima 
              yathu yowazidwa kuicotsera cikumbu mtima coipa, ndi matupi athu 
              osambitsidwa ndi madzi oyera;  
                       Funso #2 
 Yohane 14: 6-7 
              6Yesu ananena naye, ine ndinenjira, ndi coonadi, ndi moyo. Palibe 
              munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine. 
              7Mukadazindikira ine mukadadziwa Atate wanganso; kuyambira tsopano 
              mumzindikira iye, ndipo mwamuona iye.  
             1 Yohane 1: 5 
              5Ndipo uwu ndi uthenga tidaumva kwa iye, ndipo tiulalikira kwa inu, 
              kuti Mulungu ndiye kuunika, ndipo mwa iye monse mulibe mdima.  
            Aroma 3: 20-24 
              20cifukwa kuti pamaso pace palibe munthu adzayesedwa wolungama ndi 
              Debito za lamulo; pakuti ucimo udziwika ndi lamulo. 
              21Koma tsopano cilungamo ca Mulungu caoneka copanda lamulo, cilamulo 
              ndi aneneri acitira ici umboni; 22ndico cilungamo ca Mulungu cimene 
              cicokera mwa cikhulupiriro ca pa Yesu Kristu kwa onse amene akhulupira; 
              pakuti palibe kusiyana; 23pakuti onse anacimwa, naperewera pa ulemerero 
              wa Mulungu;24ndipo ayesedwa olungama kwaulere, ndi cisomo cace, 
              mwa ciombolo ca mwa Kristu Yesu;  
            Ezekieli 18:32 
              32Pakuti sindikondwera nayo imfa ya wakufayo, ati Ambuye Yehova; 
              cifukwa cace bwererani, nimukhale ndi moyo. 
            Aroma 3:23 
              23pakuti onse anacimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu; 
            Macitidwe 4:12 
              12Ndipo palibe cipulumutso mwa wina yense, pakuti palibe dzina lina 
              pansi pa thambo la kumwamba, lopatsidwa mwa anthu, limene tiyenera 
              kupulumutsidwanalo. 
            Have You Received God's Gift 
              of Salvation? 
            Funso #3 
            Yohane 6:29 
              29Yesu anayankha nati kwa iwo, Nchito ya Mulungu ndi iyi, kuti mukhulupirire 
              iye amene Iyeyo anamtuma.  
            Yohane 5:24 
              24Indetu, indetu, ndinena kwa inu, kuti iye wakumva mau anga, ndi 
              kukhulupirira iye amene anandituma Ine, ali nao moyo wosatha, ndipo 
              salowa m'kuweruza, koma wacokera kuimfa, nalowa m'moyo. 
            1 Yohane 5: 10-12 
              10Iye amene amkhulupirira Mwana wa Mulungu ali nao umboni mwa iye; 
              ye wosakhulupirira Mulungu ananuyesa iye wonama; cifukwa sanakhulupirira 
              umboni wa Mulungu anaucita wa Mwana wace. 11Ndipo uwu ndi umboniwo, 
              kuti Mulungu anatipatsa ife moyo wosatha, ndipo moyo umene uli mwa 
              Mwana wace. 12Iye wakukhala ndi Mwana ali nao moyo; wosakhala ndi 
              Mwana wa Mulungu alibe moyo. 
            Funso #4 
             Yohane 3: 1-8 
              1Koma panali munthu wa Afarisi, dzina lace Nikodemo, mkulu wa Ayuda,2Iyeyu 
              anadza kwa Yesu usiku, nati kwa iye, Rabi, tidziwa kuti Inu ndinu 
              mphunzitsi wocokera kwa Mulungu; pakuti palibe munthu akhoza kucita 
              zizindikilo zimene inu mucita, ngati Mulungu sakhala naye, 3Yesu 
              anayankha nati kwa iye, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu 
              sabadwa mwatsopano, sakhoza kuona Ufumu wa Mulungu. 4Nikodemoananena 
              kwa iye, Munthu akhoza bwanji kubadwa atakalamba? Kodi akhoza kulowanso 
              m'mimba ya amace ndi kubadwa?  
              5Yesu anayankha, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa 
              mwa madzi ndi Mzimu, sakhoza kulowa ufumu wa Mulungu. 6Cobadwa m'thupi 
              cikhala thupi, ndipo cobadwa mwa Mzimu, cikhala mzimu. 7Usadabwe 
              cifukwa ndinati kwa iwe, Uyenera kubadwa mwatsopano. 8Mphepo iomba 
              pomwe ifuna, ndipo ukumva mau ace, komavsudziwa, kumene icokera, 
              ndi kumene imuka; cotero ali yense wobadwa mwa Mzimu.  
                       Funso #5 
 Yohane 3:36 
              36Iye amene akhulupirira Mwanayo ali nao moyo wosatha; koma iye 
              amene sakhulupirira Mwanayo sadzaona moyo, koma mkwiyo wa Mulungu 
              ukhala pa iye. 
             Yohane 16:24 
              24Kufikira tsopano simunapempha kanthu m'dzina langa; pemphani, 
              ndipo mudzalandira, kuti cimwemwe canu cikwaniridwe. 
             Aroma 4: 7-8 
              7ndi kuti, Odala iwo amene akhululukidwa kusayeruzika kwao, Nakwiriridwa 
              macimo ao, 8Wodala munthu amene Mulungu samwerengera ucimo. 
             Aroma 5: 1 
              1Popeza tsono tayesedwa olungama ndi cikhulupiriro, tikhala ndi 
              mtendere ndi Mulungu mwa Ambuye wathu Yesu Kristu;  
               
              2 Akorinto 5:17 
              17Cifukwa cace ngati munthu ali yense ali mwa Kristu ali wolengedwa 
              watsopano; zinthu zakale zapita, taonani, zakhala zatsopano, 
            Aefeso 1:13 
              13Mwa Iyeyo inunso, mutamva mau a coonadi, Uthenga Wabwino wa cipulumutso 
              canu; ndi kumkhulupirira iye, munasindikizidwa cizindikilo ndi Mzimu 
              Woyera wa lonjezano, 
             Ahebri 13: 5 
              5Mtima wanu ukhale wosakonda cuma; zimene muli nazo zikukwanireni; 
              pakuti iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya 
              ndithu.  
             Aefeso 1: 3-6 
              3Wolemekezeka Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Kristu, amene 
              anatidalitsa ife ndi dalitso lonse la mzimu m'zakumwamba mwa Kristu; 
              4monga anatisankha ife mwa iye, lisanakhazikike dziko lapansi, tikhale 
              ife oyera mtima, ndi opanda cirema pamaso pace m'cikondi, 5Anatikonzeratu 
              tilandiridwe ngati ana, a iye yekha mwa Yesu Kristu, monga umo kunakomera 
              cifuniro cace, 6kuti uyamikidwe ulemerero wa cisomo cace, cimene 
              anaticitira ife kwaufulu mwa Wokondedwayo. 
             2 Akorinto 5:21  
              21Ameneyo sanadziwa ucimo anamyesera ucimo m'malo mwathu; kuti ife 
              tikhale cilungamo ca Mulungu mwa iye. 
             Afilipi 3: 8-9 
              8Komatu zeni zeninso ndiyesa zonse zikhale citayiko cifukwa ca mapambanidwe 
              a cizindikiritso ca Kristu Yesu Ambuye wanga, cifukwa ca Iyeyu ndinatayikitsa 
              zinthu zonse, ndipo ndiziyesa zapadzala, kuti ndikadzionjezere Kristu, 
              9ndi kupezedwa mwa iye, wosati wakukhala naco cilungamo canga ca 
              m'lamulo, koma cimene ca mwa cikhulupiriro ca Kristu, cilungamoco 
              cocokera mwa Mulungu ndi cikhulupiriro; 
             
             
           |