Project Hope     home >>buku lophunzitsira lotsogolera >>phunziro 1 >>phunziro 2
Buku Lophunzitsira Lotsogolera - Phunziro #2
Women's Empowerment Program
Sports Bible Club
Living Water Bible Club

Yesu anati chani?

Cholinga cha phunziro

Kufotokoza za Yesu ngati Mwana wa Mulungu pa upadeladela wake umene
ananena za Iye ndi zimene ena ananena za Iye.

• Kuzindikira mphamvu ndi uthunthu wa ziphunzitso ndi mauneneri, amene
amasonyeza anali Mulungu.

Mu maphunziro athu a baibulo a sabata ndi sabata, mafunso adzasiyana. Poti zigawo
za mbaibulo ndi zazitali ndipo amawerenga kunyumba, sizofunika kuwerenga pa
gulu. Funsani munthu m'modzi awerenge yankho. Ngati ena ali ndi yankho losiyana,
atha kuyankha. Werengani yankho loperekedwa mu buku lotsogolera ngati
mowombera nkota. Kenaka pitilizani pa gawo lililonse la Baibulo.

Pemphero

Atate wokondedwa wa kumwamba, Buku ilo munalemba ndi lamphamvu! Ndilodzala ndi
choonadi! Tikufuna tiphunzire zimene Yesu adaphunzitsa anthu. Tsegulani maso athu kuti kuti tione ndi kumvetsa mau Ake. Tapemphera mu dzina Lake lodabwitsa, ame.

Mau Otsogolera

Mu maphunziro athu apa Sabata, tikuwerenga Chiphunzitso cha pa Phiri.Titha kuyamba
maphunziro athu pakupatsirana kupereka mayankho pa gawo lathu mu Baibulo.

Werengani vesi pansipa ndipo mulembe m'mawu anu chinthu chimodzi chimene Yesu ananena kwa anthu.


Kuwerenga Baibulo kwa Sabata:

(Use your Bible or Africa Bible Verse Handbook)

Mateyu 5:1-12,
(Timasangalala pamene tikukhala m'mene Mulungu amanenera kuti tidzikhala)

Mateyu 5:13-16,
(Yesu anatiphunzitsa kuti anthu okhulupirira Iye ndi nchere ndi kuunika kwa dziko.)

Mateyu 6:1-15,
(Yesu anatiphunzitsa ife mnene tingapempherere)

Mateyu 6:24-34,
(Tisamadandaule.)

Mateyu 7:1-12,
(Tisaweruze wena. Tichitire wena m'mene ife tikangondere wina kutichitira)

Mateyu 7:13-20,
(Yesu anatiphunzitsa njira yoyenera kukhala ndi m'mene tingazindikirire aphunzitsi onyenga)

Mateyu 7:21-27,
(Tilole Yesu akhale Mbuye wa miyoyo yathu ndi kumanga miyoyo yathu pa maziko olimba a chikhulupiriro mwa Mulungu.)

Ngati gulu la mbiri silinamalize kuwerengedwa kwa Baibulo pa sabata, mutha kuwerenga ma gawo ena pomaliza pa zigawo maphunzirondipo alembe nkhani yofunsidwayo. Kupangira limodzi kutha kuwathandizira m'mene angapangire
akamaphunzira pa okha.

Tipitirira kuphunzira mayankho ku funso "Yesu ndi Ndani?" pa zimene Yesu ananena za Iye
ndi kuphunzira maina ena amene anadzicha Yekha.

Limodzi mwa maina linali "Ine ndilipo" tinatchulako dzinali mongodutsa sabata yatha. Ndidzina la Mulungu. Ine ndilipo litanthauza ali nthawi zonse, analiko nthawi zonse, ndipo adzakhala
nthawi zonse. limanditsimikizira uthunthu ndi kukhala kosamaliza."

Atsogoleri achipembedzo mu nthawi ya Yesu anafuna kumuponya miyala chifukwa anadzitcha yekha Ine ndilipo" Anazindikira Ine ndilipo kukhala dzina la Mulungu. Izi zalembedwa mu Chipangano chathu cha Tsopano." Yohane 8:56-59 . . . . .

1. Mulungu anadzivumbulutsa Yekha kwa mose ngati InGod introduced Himself to
Moses as INE NDINE AMENE NDIRI (Exodo 3:14). Kawiiri mu Uthenga Wabwino,
Yesu akudzichula kuti NDINE. Akumaliza ziganizo zimene zikuonka zosamaliza.
(NDINE…) ndi mau amene amafotokoza za chimene ali kwa iwo omukhulupirira Iye.)

Werengani ziganizozi ndipo mumalize.

a. Yohane 13:19. . . . . Ndine (Amene ndili)

b. Yohane 8:12. . . . .. Ndine (kuunika kwa dziko)

c. Yohane 10:9. . . . .. Ndine (njira)

d. Yohane 10:11. . . . Ndine (m'busa wabwino)

e. Yohane 10:36. . . . Ndine (mwana wa Mulungu)

f. Yohane 11:25. . . . Ndine (kuuka ndi moyo)

g. Yohane 6:48. . . . . Ndine (mkate wa moyo)

h. Yohane 14:6. . . . . Ndine (njira, choonadi, ndi moyo)

Jesus is the way to God. He is the truth about God He is the very life of God in those who receive Him.

Maina operekedwa kwa Yesu mu phunziro 1 ndi funso lapambuyo akuonetsera
chikhalidwe Chake.

Pa mthawi zosiya m'miyoyo yathu, maina ena aYesu ndi athanthauzo lomvekabwino
kwa ife. Mwachitsanzo, pa nthawi imene tikufuna chitetezo ndi citsogozo, dzina,
"Mbusa wa Bwino" litha kukhala la tanthauzo lalikulu kwa ife. Pamene tikuwerenga
Baibulo ndi kumadya chakudya cha uzimu, ndi "Mkate wa Moyo" wathu.

2. Ndi dzina liti limene lili ndi tanthauzo pa nyengo mukudutsa pano.. . . . . (Lolani
munthu wina aliyense ayankhe. ena atha kufuna afotokoze za m'mene dzinalo
likuthandauzira kwa mbiri kwa iwo, koma onetsetsani asalankhule kwa nthawi yayitari.)


Yesu anaphunzitsa mu njira zitatu—P a chiphunzitso chake, pa mafanizo, pa mauneneri Ake. Choyamba tiona limodzi la chiphunzitso cha Yesu.


"Chiphunzitso cha pa Phiri"

Chiphunzitso chimene Yesu analalikira Chiphunzitso ndi “Malankhulidwe opereka malangizo mu chipembedzo kapena chikhalidwe”

Marko ndi Luka analemba za chiphunzitsochi mu Uthenga Wabwino. Koma, Mateyu amene alinali m'modzi wophunzira wa Yesu analemba motambasula.Ndizotheka kuti Yesu analalikira Chiphunzitsochi, gapena gawo la ichi, kawirikawiri akamayenda mu dziko.

Sabata yatha, tikamawerenga, ndi kumaliza za funso 3, timawerenga chiphunzitso chonse cha Phiri. Nde sitiwerenganso. Onani kuchuluka kwa zinthu zimene Yesu ananena pa Chiphunzitso cha pa Phiri.


3. Werengani Chiphunzitso cha pa Phiri chodziwika bwino chimene chikupezeka pa, Mateyu 5:1-7:29. Lembani mitu ndi za Mbaibulo zili pansinzi zimene zili zopindulitsa kwa inu.

Chitsanzo:
Kuphunzitsa za kukwiya. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ..... .. . . Mateyu 5:21-26

Mayankho:
Chimwemwe chenicheni. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ........ . . . . . .Mateyu 5:3-12
Nchele ndi Kuunika . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ..... . . . . . .Mateyu 5:13-16
Chiphunzitso cha Chilamulo. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ...... . . . . . .Mateyu 5:17-20
Chiphunzitso cha chigololo. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .... . . .. . . .Mateyu 5:27-30
Chiphunzitso cha kusudzula. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .... . . . . . .Mateyu 5:31-32
Chiphunzitso cha pangano. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .... . . . . . . .Mateyu 5:33-37
Chiphunzitsochobwezera. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. ... . . . . . . .Mateyu 5:38-42
Kukonda adani . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. . . ... . . . . . .Mateyu 5:43-48
Chiphunzitso cha Chikondi. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ........ . . . . . .Mateyu 6:1-4
Chiphunzitso cha Pemphero. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. .. . . ..... . . . . . . .Mateyu 6:5-15
Chiphunzitso cha Kusala. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... . . . . . . .Mateyu 6:16-18
Chuma Kumwamba. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... . . . . . . .Mateyu 6:19-21
Nyali ya thupi. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... . . . . . . .Mateyu 6:22-23
Mulungu ndi Chuma. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... . . . . ... . . . . . .Mateyu 6:24-34
Kuwereza Ena. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. . .. . . . ........ . . . . . .Mateyu 7:1-6
Funsa, Funa, Gogoda. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... ...... . . . . . .Mateyu 7:7-12
Khomo lopapatiza. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. . . ..... . . .Mateyu 7:13-14
Mtengo ndi zipatso zache. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... . . . ... . . . .Mateyu 7:15-20
Sindikudziwani. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . ... ... . . . .Mateyu 7:21-23
Omanga nyumba awiri. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. . . . .... . . .Mateyu 7:24-27
Ulamuliro wa Yesu. . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . . .. . . . . . . . . .. . . Mateyu 7:28-29)

Yesu amaphunzitsa m'mafanizo.

Fanizo lomwe Yesu ananena

Fanizo ndi kankhani kakafupikamene kamafotokoza za uzimu ndi chikhalidwe.


Amagwiritsa ntchito zitsanzo zimene amazitenga kuchoka ku
chilengedwe ndi ku zinthu zochita pa moyo wa tsiku ndi tsiku kuti afotokoze choonadi cha
chikhalidwe ndi cha uzimu.

Mu Baibulo fanizo linali ndi tanthauzo lobisika limene limafunika kufotokozeredwa. Yesu amagwiritsa kanenedweka kuti abise tanthauzo kwa adani ake. Pa chifukwa ichi, iwo ofuna kumukola amakanika kupeza choyankhula chatchutchutchu kuti
achigwiritse ntchito pomukola.

Chomodzi chosangalatsa ndi mafanizo ndichakuti amapereka choonadi cha mphamvu mu njira yochititsa chidwi, imene anthu omvera samadzidzimukiratu panthawiyo.

Baibulo limatiphunzitsa angamvetse ndani zimene Yesu ananena. Mtumwi Paulo amati chani za ichi pa 1 Akolinto 2:13-16? . . . . . Iyi imati anthu amene alibe Mzimu wa
Mulungu mwa iwo sangamvetse zimene Yesu ananena. Mau ake amaoneka achabechabe
kwa iwo omwe sali Akhristu.

Ophunzitsa Baibulo Charles Ryrie anati choona chophunzitsidwa mu Baibulo ndi zinsinsi,
chifukwa sizinavumbulutsidwe mu Chipangano cha Kale. Zinavumbulutsidwa ndi Khristu mu
Chipangano Chatsopano kwa iwo anaika chikhulupiriro mwa Iye.

Mu funso 4, tikupeza mafanizo asanu ndi awiri kuchokera ku Mateyu 13. Mungakonde
kuwerenga funso lotsatira ndi kunene choyamba?

4. Patsiku lina. pambali pa mtsinje, Yesu analalikira chiphunzitso cha mphamvu
chimene chili ndi mafanizo asanu ndi awiri. Tsekulani tsamba 34-38 ndipo werengani
ulalikiwu—Mateyu 13:1-58. Werengani maina a mafanizo asanu ndi mu gawo ili:

1. (odzala)
2. (namsongole)
3. (njere ya mpiru)
4. (chotupitsa mkate)
5. (chuma chobisika)
6. (khola)
7. (khoka)

Ananenera za Iye, pamodzi, Yesu ananena mafanizo 60 amene analembedwa mu Uthenga Wabwino. Ena amabwerezedwa mu mauthenga ena abwino. Imodzi yodziwika bwino ndi fanizo la Ofesa.

5. Mateyu, Marko, and Luka ikunena za matambasulidwe a Yesu pa fanizoli.
Werengani Luka 8:11-15 . . . . .

a. Kodi wofesa amadzala chani? . . . . . (Mau a Mulungu)

b. Chimene chimalepheretsa ? . . . . . (Satana amalanda, mau sakhazikika; mavuto
akabwera timazisiya; nkhawa za moyo uno, ndi chikondi cha chuma zimawatsamwitsa.)

c. Chifukwa chani nthaka ina imapindura kusiyana ndi yina?. . . . . (Ndi nthaka ya
bwino— anthu amamva mau a Mulungu, kuwamvetsetsa, kuwakhulupirira, ndi
kuwamvera.)


Kulimbikitsa gulu kuti ligawane, mutha kuyamba ndi kupereka mayankho anu ku funso 6.
Limbikitsanani kulingalira zosintha.


6. Lingalirani za fanizo lanthaka.

a. Ndi nthaka yanji imene moyo wanu ukuyimira?. . . . . (Mafunso asiyana.)

b. Ndi kusintha kwa ntundu wanji komwe kukufunika kuti moyo wanu usinthe
ndikukhala nthaka ya bwino.. . . . (Mafunso asiyana.)

Tsopano tiona ma uneneri ena a Yesu.

Mauneneri amene Yesu ananeneratu

Uneneri umachokera "pakuyankhula motsogozedwa ndi Mulungu"

Pa Phunziro 1, timawerenga za mauneneri a aneneri a Chipangano cha kale amene ananena za kubwera kwa Yesu ndi m'mene mauneneriwo anakwaniritsidwira. Kodi mukudziwa kuti Yesu Khristu anatipatsa mauneneri?

Ananeneratu za kukanidwa ndi Petulo, kukanidwa ndi ophunzira ake, kukumana ndi ophunzira ake mu Galileya idadutsa nthawi yakufa ndi kuuka kwake ndi kubwera kwake kwa chiwiri.

Werengani Funso 7, imene imabvumbulutsa ena mwa mauneneri.

7. Chipangano cha Tspopano chili ndi ma ulosi ambiri a Yesu. Ochepa ndi awa ali
pansipa. Lembani fundo ya Baibulo yolondola.

Marko 8:38
Marko14:72
Luka 24:5-7
Yohane 5:25-29
Yohane 12:32-33

Za m'Baibulo

a. Kukanidadwa ndi ophunzira ................................(Marko 14:72 . . . . .)
b. Imfa yake............................................................... (Yohane 12:32-33 . . . . .)
c. Chiukitso Chake.................................................. (Luka 24:5-7 . . . . . )
d. Chiukitso chathu ..................................................(Yohane 5:25-29 . . . . .)
e. Kubweranso kwake ............................................(Marko 8:38 . . . . .)

Ngati gule lingafunse “—nthaw yakwana—” pa Yohane 5:25-29, Ikunena kuti Yesu amanena nthawi imene anautsa Lazalo kwa akufa. (Yohane 11:17-44).

Yesu ananenea za mbiri za masiku otsiriza. Tsegulani pa Mateyu 24:1-3. . . .
Kodi ndi mafunso awiri ati omwe ophunzira anafunsa Yesu?.What two questions did the
disciples ask Jesus? . . . . . (Kodi kachisi adzagumulidwa liti? Kodi chizindikiro choti Yesu akubwera chidzakhala chotani?)

Ulosi wa kachisi unakwaniritsidwa mu chaka cha A.D. 70—zaka 37 kuchokera mu nthawi imene Yesu anali pa dziko lino.—pamene Aroma "anaonongeratu Yerusalem ndi kachisi [ndipo] miyala inaikidwa kuti idzitunga golide amene amatayikira pansi."

Yesu anayankha funso lachiwiri. Tsegulani Mateyu 24:36-39. . . . . Yesu, mu
umunthu wake, ananena palibe koma ndi Atate okha amene akudziwa tsiku lakubwera
kwake.Tisakhulupirire anthu amene amayika masiku akubwera kwa Yesu!

Yesu anati zambiri zidzachitika asanabwere. Takhala ndi chilala, zibvomerezi, ndi zigumula. Koma izi zidzachitika mowirikiza ndi mwamphamvu pamene Yesu wayandikira kubwera.

Tikadziwa Yesu ngati mpulumutsi, titha kumukhulupirira za tsogololathu.
Tisasiye phunziro limene Yesu ananena posaphunzira gwero la mau ake.

8. Mau amene Yesu amayankhula amachoka kuti?
Yohane 17:5-8 . . . . . (Tate)

Onani Yesu anati zonse zimene anena zikuchoka kwa Atate Ake. Tsopano tatsimikiziridwa mau ake ndi choonadi. Zonse zimene Yesu ananena ndi kuchita zimachoka kwa Mulungu, Atate ake.

Ngakhale adani aYesu, alonda ogwira ntchito kwa Asembe akuluakulu ndi a pharisi, anasangalatsidwa ndi zimene Yesu amanena. Onani Yohane 7:45-46 . . . . .
Zinali zoona. Palibe analankhula ngati m'mene Yesu amalankhulira!

Mu chipangano cha Kale timawerenga nthawi zimene Mulungu analankhula kwa
aneneri, asembe, ndi mafumu. Baibulo linalemba izi kunena " Baibulo linanena izi kuti
"Mulungu anati......kapena Mau a Mbuye anabwera........" Mulungu analankhulanso
kwa anthu mu chipangano chatsopano.

9. Kwa ndani kumene Mulungu anapereka mau Ake ndi uthenga mu Chipangano cha
Tsopano munsimu?

a. Marko 1:10-11. . . . . (kwa Yesu )
b. Yohane 1:32-33 . . . . . (Yohane mbatizo)
c. Machitidwe 11:4-9 . . . . . (kwa Peturo)

Mulungu analanhkula mu njira zina kwa anthu ena. tsegulani tsamba 330 mu Chipangano
chanu cha Tsopano ndikupeza Machitidwe 10:3-6. Tiuzeni m'mene Mulungu analankhulira
ndi Korneliyo.. . . . . (kudzela m'masomphenya angelo). Pano, Mulungu akuyankhula ndi wa a mitundu, zimene zinadabwitsa Ayuda. Amaona ngati Mulungu amayankhula ndi Ayuda okha!

Pamene atsogo;eri a mpingo wa ku Antiokeya amatumikira Ambuye, ndi kusala kudya,
Mulungu analankhula nawo bwanji? Machitidwe 13:2-3 . . . . . (mwa Mzimu woyera).
Mulungu amalankhula nawo mwa Mzimu woyera. Anawauza atumize Sauli, amenenso ali ochedwa Paulo, ndi Barnaba ngati atumwi kwa Amitundu.

Mulungu amayankhulanso kwa ife lero. Werengani Aheberi 1:1-2a. M'mau anu izi zitanthauzanji? . . . . (Mulungu amayankhula nafe kudzera mwa mwana wake, Yesu)

Tangoganizani! Mulungu amayankhula ku mitima yathu nthawi zonse tikamaewerenga
Baibulo. Mbali yathu ndi kumverea ndi kuchita.
Muwerenge Miyambo 8:34-35. . . . .

Mulungu akulankhula ndi anthu lero. Tikamva uthenga ochokera ku mau a Mulungu,
timadziwa Mulungu akuyankhula nafe. Werengani 1 Atesolonika 2:13 mu
chipangano chanu Chatsopano.. . . . .

Mulungu watiuza kale zonse zimene tikuyenera kudziwa za moyo-kumbuyo, panopa, ndi
kutsogolo. Wasungu Buku lake mu mibado mibado ndipo wasunga zolemba zoyambirira. Kodi sizopatsa kaso kuti tikuwerenga malingaliro a Mulungu m'mau ake?

10. Mwaphunzira chani za Yesu ndi zimene anachita. . . . . (Lolani wina aliyense anene
yanho lake.)

Kudzera mu kuona Baibulo, taphunzira Yesu ndi Mulungu. Amachedwa Mwana wa Mulungu.
Zonse ananena pozoyankhula Zache, muziphunzitso Zache, mu mauneneri Ake, mu mafanizo Ake, ndi mauneneri ake amachoka kwa Mulungu. Tikudziwa zonse Yesu ananena ndi zoonaChoona cha Mulungu.

Sabata ya mawa, phunziro lathu likutchedwa 'Yesu Anapanga Chani?" Tidzaphunzira kufunika ko gwira ntchito ndi kupumula.

Pa phunziro 3 mpaka 6, mudzalemba pemphero lanu kutseka nthawi yowerengera ku
nyumba. Izi zikupatsani danga loyamika Ambuye ndikumufunsa akuthandizeni kuchita
choonadi cha Baibulo pa moyo wanu. Pemphero lanu silidzagawidwa pa gulu.

Pemphero lotsekera

Ambuye Yesu, zikomo tikudziwa zonse zimene munanena ndi zoona. Palibe analankhula ngati Munalankhulira. Titha kudalira malonjezano Anu. Zikomo potiphunzitsa. Tapemphera mu dzina Lanu, ame.

 
 

 

YESU NDI NDANI?

Buku Lothandiza

 
 
Copyright ©  2023 www.UnitedCaribbean.com. All rights reserved. Disclaimer Click to Contact us