Project Hope     home >>buku lophunzitsira lotsogolera >>phunziro 3 >>phunziro 4
Buku Lophunzitsira Lotsogolera - Phunziro #4
Women's Empowerment Program
Sports Bible Club
Living Water Bible Club

Chifukwa chani Yesu anabwera?

Cholinga cha Phunziro

• Kuzindikira kuti zotsatila za tchimo ndi imfa.
• Kuzindikira kulephera kwa munthu kudzilipirira Yekha dipo.
• Kuphunzira chifukwa chimene Yesu anasiya ulemerero wa kumwamba ndi kubwera ku dziko lino lauchimo.
• Kuzindikira kufunika kwa Infa ya Yesu ya pa mtanda.

Limbikitsani gulu kuganizira wena amene angawalimbikitse kuti azibwera ku
maphunziro a Baibulo, amene ayambe m'masabata ochepa akubwerawa.

Zofunikira! Ngati wina wafunsa m'mene angakhalire Mkristu, mukhale okonzeka
kuyankha. mutha kufotokoza dongosolo ya chipulumutso, osachititsa manyazi
wina. Perekani mwayi kuti munthu apemphere alandire Yesu.

Pemphero

Wokondedwa Atate a Kumwamba, zikomo pa zonse matiphunzitsa za Mwana Wanu, Yesu
Khristu. Tikufuna tidziwe nchifukwa chani anabwera ku dziko la pansi. Tiphunzitseninso
kuchokera m'mau anu. Tapemphera mu dzina la Yesu, ame.

Ndemanga zotsogolera

Kodi munazindikirapo ichi kuti mutha kudziwa maganizo a mMulungu kuchokera mu Buku
limene anatipatsa? Titha kudziwa zimene Mulungu amagzaniza pa zosiyanasiyana
chifukwa watiuza mu Buku lake lodabwitsa. Choti tichite ndikungolitenga ndi kuliwerenga.
Ndizimene tikuchita pa maphunzirowa—kutenga maganizo a mulungu m'moyo mwathu.

Pa mayambiriro a phunziro lililonnse, tapatsidwa magawo a Baibulo oti tiwerenge amene
ali ogwirizana ndi phunziro. Kuwerenga Baibulo ndi kupemphera itha kukhala nthawi
yabwino yoyanjana ndi Mulungu, chifukwa tikuwerenga ndi kumva Malingaliro a Mulungu.
Tsopano tiwerenge kuyankha kwathu mu kuwerenga kwathu kwa sabata ino.

Kuwerenga Baibulo kwa Sabata:

(Use your Bible or Africa Bible Verse Handbook)

Werengani gawo la Baibulo pansipa ndipo mulembe m'mau anu zimene limanena
za chifukwa chimene Yesu anabwerera ku dziko lapansi.

Mateyu 5:1-2, 17-20
(Yesu anati anabwera kudzapanga chiphunzitso cha Chipangano cha Kale kuti chikhale choona.)

Yohane 6:35-38
(Yesu anabwra kudzapanga chifuniro cha Atate)

Machitidwe 2:23-24
(Yesu anabwera kudzafa ndi kuukutsidwa. Mulungu anakonza kuti Yesu apereke moyo Wake ndi kuukitsidwa kwa akufa)

1 Yohane 3:5-6
(Yesu anawoneka kuti achotse tchimo.)

Aheberi 2:14-15
(Imfa ya Yesu inawononga satana ndi imfa.)

Chibvumbulutso 3:20-21
(Yesu akugogoda pa khomo pa mitima ya anthu, kuti akapereke chigonjetso kwa iwo amuitana Iye miyoyo yawo.)

Chibvumbulutso 5:9-10
(Imfa ya nsembe ya Yesu idzabweretsa anthu ochokera ku mtundu, chiyankhulo, fuko ndi mtundu wonse kutumikira Mulungu.)

Taphunzira chani panopa? Mu phunziro loyamba, taphunzira kuti Yesu anali ndi maina
ambiri. Ndi dzina liti lomwe lili ndi tanthauzo lofunika kwa inu. lero . . . .?

Maina ambiri akutikumbutsa kuti Iye ndi Mulungu ndi amodzi. Tapeza kale maina awiri a
mainawo. Mukuwakumbukira? Akupezeka pa Yesaya 9:6 . . . .?
Ali Mulungu wankulu ndi Tate Wosatha.

Pa phunziro 2, taphunzira zinthu zina zimene Yesu anaphunzitsa mu Ziphunzitso zonse,
mafanizo, ndi mauneneri. Amatiphunzitsa m'mene tingakhalire m'moyo wa umulungu—
Moyo umene umamusangalatsa Mulungu ndi munthu.

Mu phunziro 3, taona Yesu akuchita zozizwa. Amachilitsa iwo amene ali wodwala. Tsiku
ndi tsiku amayangana ndi chifundo iwo amene anali osautsidwa ndipo amawapatsa
zosowa zawo. anaukitsa akufa, kutulutsa ziwanda, kubwezeretsa ziwalo zakufa,
ndikudyetsa makamu a wanthu modabwitsa.

Aneneri ananenera Mulungu adzabwera ndi kuwapulumutsa. Atsogoleri a chipembedzo,
amene amadziwa za Chipangano cha Kale uneneri wa Yesaya, amayenera kudziwa chimene Yesu anali pamene anamuona akuchiritsa anthu. Tsegulani limodzi la mauneneri wa Yesaya pa mamalizilo a buku ili. Yesaya 35:4-6 . . . . .

Mu phunziro lathu, tiphunzira chifukwa chimene Yesu anabwerera. Sanabwere kudzalalikira ziphunzitso zikulu zikulu kapena kudzachilitsa anthu. 37
Chifukwa chain anabwera pa dziko lapansi? Baibulo pa funso 1 likutipatsa zifukwa zimene Iye anabwerera.

1. Chifukwa chani Yesu anabwera pa tdziko la pansi? Baibulo likutipatsa zifukwa
zambiri pansipa.

a. Mateyu 5:17. . . . . (kupangitsa ziphunzitso za Mulungu zoona)

b. Yohane 1:18. . . . . (kuonetsera Mulungu kwa anthu)

Yesu ndi Mulungu komanso munthu. Ndizosangalatsa kuti amatchedwa mwana wa Mulungu komanso mwana wa munthu. —kuonetsa umulungu wake ndi umunthu wake.

c. Mateyu 20:28 . . . . . (kupulumutsa ndi kupereka moyo wake kuti anthu apulumutsidwet)

d. Luka 4:42-43. . . . . (kulalikira Uthenga wa Bwino wa Ufumu wa Mulungu)

e. Luka 19:10. . . . . (kupulumutsa ndi kufunafuna chotayikacho)

f. Yohane 3:17. . . . . (kukhala Mpulumutsi wa dziko)

g. Yohane 10:7-10. . . . . Onani vesi 10. (kupereka kwa okhulupirira moyo wodzala mu kuchuluka kwake)

h. 1 Timoteyo 1:15. . . . . (kupulumutsa ochimwato)

Ma vesi ambiliwa akukamba zinthu zimodzi mosiya. kuombera nkota, ma vesiwa amati
chani za chifukwa chimene Yesu anabwerera?. . . . . (Yesu anabwera kuzakhakla mpulumutsi wathu) Tikufunika mpulumutsi chifukwa ndife ochimwa.

Baibulo limati Mulungu analenga angelo ndi anthu mkuwapatsa chisankho chosankha
chabwino kapena choyipa. Ngati sitisankha Mulungu tachimwa.

Satana, wokongola, ngelo wa mphamvu, anali woyamba kuchimwa. mu kudzikuza kwake
amafuna kutenga malo a Mulungu. Yesaya 14:12-14, ikufotokoza maonekedwe a kudzikuza a satana ndi m'mene anachokera ku mwamba........Satana atachimwa kumuchimwira Mulungu, anamnyenga Adamu ndi Hava kuti asamvere Mulungu. Hava ananyengedwa ndi satana koma koma adamu adasankha kusamvera.
Werengani Aroma 5:12 . . . . .

Kuyambira nthawi imeneyo, munthu yense amene anakhalapo anachimwa.
Angakonde kuwerenga zimene Baibulo linanena ku Aroma 3:23

“Yese wachimwa ndi kutalikilana ndi kupezeka kopulumutsa kwa
Mulungu.”

—Aroma 3:23

Chilango cha uchimo chinalengezedwa ndi Mulungu kwa Adamu ndi Hava pa chiyambi. Chilango chinali cha imfa ya kuuzimu ndi kuthupi. Genesis 2:17 ikuti, “Koma mtengo wa kudziwitsa chabwinio ndi choyipa musadye, pakuti tsiku limene mudzadya mudzafa.

Werengani Aroman 6:23


“Pakuti tchimo lili ndi dipo lake—imfa; koma mphatso ya ulele ya
Mulungu ndi moyo wosatha mu ubale ndi Khristu Yesu Mbuye wathu.”
—Aroman 6:23

Pali njira imodzi imene tingapulumutsidwire? Machitidwe 4:11-12 . . . . .

Komanso, chifukwa chani tikufuna Mpulumutsi?. . . . . (chifukwa tamuchimira Mulungu)

Tamuchimwira Mulungu. Tatsutsana naye ndi kusankha kukhala osiyana ndi Iye. zimenezo
ndi uchimo. Chifukwa chake tikufuna mpulumutsi.—kutipulumutsa ku dipo la tchimo.

Yesu ndi mlowa malo wathu

Kuyambira ku Chipangano cha Kale, mulungu amavumbulutsa kuti mlowamalo
wosalakwa, wosachimwa afe chifukwa cha tchimo la wina. koma tangowerenga
Aroma 3:23, imene ikuti onse anachimwa. Sipanakhaleko munthu ochimwa,
kupatulako Yesu Khristu.

Chifukwa chimene anabwerera ku dziko la pansi. anabwera kudzakhala mlowa m'malo
wosalakwa. panalibe njira ina imene tikanakhululukidwa! Yesu anayenera kubwadwa mwa
namwali, kuti askhale ndi chikhalidwe cha tchimo la Adamu—chimene anthu onse
anayamwira. anakhala m'moyo wosachimwa ngati mwana, m'nyamata, ndi wankulu.

Titha kuwerenga chikhalidwe chopanda uchimo cha Yesu pa 2 Akorinto 5:21 mu mabuku athu ophunzirira. . . . . .

“Khristu analibe tchimo Christ . . . .”
—2 Akolinto 5:21


Yesu ali ndi zaka 30, anayamba utumiki wake pa dziko lino. Panthawiyo adabatizidwa
ndipo Mulungu analankhula kumwamba kunena kuti akondwera ndi moyo wa Yesu ndi
zonse anachita. Werengani izi Marko 1:11. . . . . (Mulungu anati, “Ndikondwera nwawe.”)

2. Yesu ananeneratu momveka bwino kuti adzaphedwa ndi kuuka kwa akufa.
Anawuza yani, ndipo anawawuza chani tikawerenga pansipa?

a. Luka 18:31-33 . . . . . (Yesu anauza ophunzira kuti adzaperekedwa kwa amitundu. Anafotokoza za chimene adzachitidwe asanaphedwe)

b. Mateyu 12:38-40 . . . . . (Anauza adani Ake, aphunzitsi a chilamulo ndi afarisi, adzaikidwa m'manda masiku atatu.)

c. Marko 8:31-32a . . . . . (Anauza ophunzira adzaphedwa ndipo akatha masiku atatu adzauka)


Munaona kuti vesi 32 Yesu ananeneratu izi kwa iwo? komano mochulukir anthu
amamulondola Yesu, mochulukira atsogoleri a chipembedzo ndi afalisi amamukana ndi
kumusautsa. Koma nthawi inafika yoi aYeus aperekedwe ndipo anagwidwa. Koma tiyeni tiwerenge ngati adani ake akanatha kumuwereza Yesu.

3. Kodi adani a Mulungu akanampeza Iye olakwa? Luke 23:4 . . . . . (Ayi)

4. Poti Yesu sanachimwepo kapena kuphwanya lamulo lililonse, chifukwa chani
anaweruzidwa kuti afe. Marko 14:61-64 . . . . . (Anaweruzidwa kuti afe chifukwa anali Mesiya, mwana wa Mulungu.)

Zinali zoona kuti Yesu ndi Mesiya Mwana wa Mulungu. Olamulira amati choona ndi chabodza anamuweruza Iye amene anali Mlengi.

Yesu sanadzikire kumbuyo. Anabwera kudziko kudzafera machimo a wena.
Kuperekedwa, kuweruzidwa ku bwalo la milandu, kukwapulidwa, ndi kukhomedwa pa
mtanda zizinali zodabwitsa kwa Iye. Zosenzi zinanenedwa zaka zambiri kumbuyoku.

Yesu amadziwa zonse izi zidzachitika. Dzilko lisanalengedwe., Anakonza kubwera
ku dziko kufa ngati Mlowa malo wa munthu. Iyi inali njira yokhayo imene anthu
akanapulumutsidwira kuchoka ku zotsatira za tchimo. Yesu anadziwa mazunzo
amene amayenera kudutsamo.

Werengani mauneneri okhudza Iye mu Yesaya 53:3- 6. . . . .

5. Pa zomangidwa zonse, imfa, ndi kukwiriridwa kwa Yesu, kuyamba pa
Marko 14:43–15:47.

Izi zinalembedwa M'mauthenga Abwino onse anayi. Wolemba wina aliyense
akutsindika zinthu zosiyana malingana ndi m'mene amawonera. mu zolemba zina,
timaphunzira kunali ziweruzo zambiri chifukwa kunali kovuta kuti amuweruze pa
chinthu choyipa. Timaphunziranso zina zimene Yesu ananena pa mtanda.

Mateyu analemba zinthu kwa zimene anthu a Chiyu amafuna kumva (Mateyu 27:27–28:15). Analemba za boma kutumiza asilikali kukatseka manda. Mateyu akufotokoza izo zidzchitika pamene Yesu anawuka kwa akufa.

Yohane anakamba zambiri za anthu amene Yesu anakamba nawo atauka kwa akufa.Anafotokoza za boma kutumiza asilikali kukatseka ndi kulondera manda. (Yohane 19:16-21:25).

Luka analemba ma buku awiri, Uthenga wa Bwino wa Luka ndi buku la Machitidwe.
Mu ma buku onse. (Luka 23:26–24:52 and Machitidwe 1:1-11), anafotokoza za m'mene Yesu anatengedwera ku mwamba masiku makumi anayi atatha chiukireni kwa akufa.

Yeus ananyamula machimo athu pa Iye Yekha. Ananyamula machimo anthu onse a munthawi zonse. Werengani 2 Akolinto 5:21 . . . . .

Satana, mdyerekeezi, ndiwogonjetsedwa chifukwa cha imfa ndi kuuka kwa Yesu.
Werengani zomwe zabvumbulutsidwa 1 Yohane 3:8-10 . . . . .

Mutha kufunsa, "Ngati satana wagonjetsedwa, chifukwa chani lero ali ndi mwayi ochita ntchito zache? Amapambana pa zifukwa zitat.

1) Anthu amasankha kumvera satana osati Mulungu.

2) Akhristu sazindikira satana ndi wogonjetsedwa, Mulungu waapatsa mphamvu zokhala
ndi moyo wa chigonjetso. Timawerenga izi pa Aefeso 1:18-22 . . . . .

3) Kugonjetsedwa kwa satana kunawoneretsedwa pamene Khristu anawuka kwa akufa.
Satana ali ndi ufulu wochita zinthu mpaka Yesu adzabwere. Satana adzalandila chilango
pamathero. Buku la Chibvumbulutso limanena nthawi yache pa Chibvumbulutso 20:1-3, 7-10, ngati mukufuna kaoneni zimenezo kunyumba.

Yesu anabwera koyamba kudzatipatsa chipulumutso. Akubweranso kudzapereka chiweruzo.

6. Baibulo limaphnzitsa momveka bwino Yesu anabwera pa dziko ndi kufa m'malo mwako chifukwa cha machimo ako. poti Yesu anafa chifukwa cha iwe, yankho lanu lidzakhala lotani? . . . . . (Mutha kufunsa munthu wina aliyense payekhapayekha kuti apereke yankho ku funsoli.)

7. Lowezani Machitidwe 4:12.

Lembani Machitidwe 4:12 pano. (Chipulumutso chimapzeka mwa iye yekha basi, pa dziko lonse palibe amene Mulungu wapereka kuti atipulumutse.)

Phunziro ya sabata ya mawa ndi l;osangalatsa kwambiri. tidzaphunzira za chozizwa
chachikulu chomwe sichinachitikepo.

Poti pemphero pa funso 8 ndi lamunthu payekha, sizofunika kuti anene. pitani ku
pemphero lotseka.

8. Uzani ambuye kuti ndinu ayamika bwanji kuti Iye amakukondani ndipo
anakuferani pa mtanda kulipira dipo la tchimo lanu. Lembani pemphero lanu apa.

Pemphero Lotsekera

Tikuyamikani, Atate wa kumwamba, chifukwa cha chiplumutso munapereka kwa ife.
Zikomo chifukwa cha chikondi chanu . Tikuthokozani Atate kumwamba, chifukwa cha
chipulumutso mudapereka kwa ife. zikomo chifukwa cha chikondi chanu
chosasinthasintha pa ife ngat anthu. Tiphunzitseni tichite zonse mwatiphunzitsa pa moyo
wathu. Tapemphera mu dzina la mphamvu la Yesu Khristu, ame.

 
 

 

YESU NDI NDANI?

Buku Lothandiza

 
 
Copyright ©  2023 www.UnitedCaribbean.com. All rights reserved. Disclaimer Click to Contact us