Project Hope     home >>stonecroft>> yesu ndani? >>phunziro 1
Stonecroft - YESU NDI NDANI?- Phunziro #1
Women's Empowerment Program
Sports Bible Club
Living Water Bible Club

Baibulo limati
Chani za Yesu?

Yesu ndi Ndani?

Sauli, munthu wachiyuda amene amamanga ndi kupha akristu oyambirira, anafunsa funso lofunikira. Ndifunso lofunikira limene tingafunse. Anafunsa, "Ndinu ndani, Ambuye?"

Analandira yankho pompopompo "
Ndine Yesu amene ukumulondalonda..."
(Machitidwe 9:5).

Munthu waukaliyu (amene anapamgitsa chipolowe mu chalitchi choyambirira ku Yerusalem) analandira uthenga woyenera, anakhala munthu wosandulika. Anali atatakasidwa ndi chikhulupiriro chabodza. Ankaganiza kuti anali kukondweretsa Mulungu pochita ntchito zake zakupha, koma iye amkalondalonda Iye.

Timachita zomwezo, pamene tikukhulupirira zinthu zimene zili zabodza. Timachita zinthu zimene zili zoyipa kwa ife eni—nkhakhalenso kwa anzathu. Njira yokhayo kuti tikhale ndi chidziwitso chenicheni ndi kuzindikira ndi kukhulupirira choonadi. Maphunziro a Baibulowa akumana ndi chosowa chanu cha choonadi. Akukankhirani ku chitsime cha zoonadi zonse, Mau a Mulungu. Mulungu akuti,

“Thambo ndi dziko lapansi zidzachoka,
koma mau anga sadzachokaHeaven.”

—Mateyu 24:35

Mau a Mulungu ndi oona ndipo adzaima mpaka kalekale. Anthu ali ndi zidziwitso zolakwika za Yesu.

People have many incorrect and strange ideas about Jesus. Since our behavior is influenced and motivated by what we believe, it is important that we have accurate information about who Jesus is, who God is and who we are. When you have finished this study, you will know beyond a shadow of a doubt who Jesus really is.

Mumakhulupirira kuti Yesu ndi ndani? Lero timamva maganizo osiyanasiyana. Ena amati ndiye amene anayambitsa chipembedzo....mtsogoleri wa nkulu wa chikristu...mphunzitsi wa nkulu wa chikhalidwe...munthu woyamba kuzunzidwa mwankhanza mum'bado wake.

Titha kudziwa zoona pokhapoka tikakhulupirira uthenga wochokera ku chitsime cha choonadi. Pali choonadi chimodzi—Mulungu. Watipatsa ife Buku, limene limatiuza m'mene tingamudziwire Iye komanso m'mene tingakhalire moyo womusangalatsa Iye ndi ife.

Yesu sali ngati m'modzi wa atsogoleri a chipembedzo pa dziko la pansi. Sali ngati munthu wankulu wa m'Baibulo ngati Abraham, Mose, kapena Davide. Nthawi zonse tikamalemba tsiku kapena chaka, timazindikira kuti zaka zikwi ziwiri (2000) zapitazo Yesu Khristu anabwera ndi kugawa mbiri m'magawo awiri:

Baibulo limatiuza zinthu zambiri zodabwitsa za Yesu. Mwachitsanzo, Yesu analipo chikhalire nthawi isanayambe. Malo ambiri mu Baibulo amafotokoza Yesu analipo pachiyambi dziko lisanalengedwe.

Baibulo limati,

“Ndipo Iye ali woyamba wa sonse. . .”
—Akolose 1:17


Yesu analipo asanabadwe ngati munthu. Wakhala ali chikhalire ndipo adzakhala mpaka muyaya. Palibe mtsogoleri wa chipembedzo amwene ananena kuti adzakhala muyaya, koma Yesu ananena. Anati,

“ . . . Asanayambe kukhala Abraham ndipo 'Ine ndiripo'.”
—Yohane 8:58

Izi zitanthauza Yesu analipo. INE AMENE NDILI ndi dzina la Mulungu.

Pa Exodo 3:14, zaka zikwi ziwiri Yesu asanabadwe, Mulungu anadzionetsera Yekha kwa Mose ngati "INE AMENE NDILI" Muchiheberi dzinali litanthauza kukhala kwa chikhalire.

Yesu anaziyerekeza Yekha ndi Mulungu (Yohane 5:18)

Kuzindikira Choonadi

Ganizani mozama ndi mwapemphero za maphunziro mukuphunzirawa.
zifunseni mafunso awa:

Baibulo pa gawo ili likuti chani?
Zindikirani choona cha Mulungu

Baibulo pa gawo ili likuti chani?
Mvetsetsani chimene Mulungu akunena.

Mulungu akundilankhula chani?
Chitengeni choonacho muchichite pa moyo wanu.

Mwapempero lingalilani m'mene Mulungu akufunira kuti Muyankhe

Muvera lamulo kapena kusintha m'mene mumaonera zinthu?

Uthenga wa Bwino

Mabuku oyambirira a Chipangano cha Tsopano sanalembedwe kukhala a mbiri ya Yesu. analembedwa ndi anthu osiyanasiyana kwa magulu osiyanasiyana ndi zifukwa zosiyanasiyana. mabuku amenewa amatchedwa uthenga wabwino.

Awiri amabukuwa—Uthenga Wabwino wa Mateyu ndi Uthenga Wabwino wa Yohane—unalembedwa ndi anthu awiri amene anayenda ndi Yesu kwa zaka zitatu. anali mu gulu la anthu khumi ndi awiri amene Yesu adawasankha ngati atumwi. Pa mu chipangano cha Tsopano pali mndandanda wa mau amene akupereka tanthauzo la mau amene simukuwadziwitsitsa. Onani tanthauzo la mtumwi. . . . .

Kuyambira pa ndi gawo losonyeza maphunziro. izi zimathandiza mukafuna kufufuza kuchoka mu Baibulo za phunziro limene mukufuna kuphunzira. Mateyu adalemba uthenga wa bwino wa Mateyu kutsimikizira a Yuda kuti iye ndiye Mesiya amene adakhala akumufunafuna.

Yohane adalemba uthenga wabwino wa Yohane kutsimikizira owerenga kuti Yesu adali Mwana wa Mulungu.

Uthenga wa bwino wa Mariko udalembedwa ndi mnyamata Maliko, amene adagwira ntchito ndi Paulo komanso Barnaba ndi Petulo. Marko adalemba kwa amitundu kuwauza za Yesu ndi zimene adachita.

Uthenga wa bwino wa Luka udalembedwa ndi dotolo wa chihelena amene anapanga kafukufuku ndi ku fusa anthu amene anali kumudziwa Yesu.

Chifukwa uthenga wabwino uluonse umalembedwa kwa anthu osiyanasiyana, onsewo amayimira mbali zosiyana za moyo wa Khristu.


1. Yohane anati chani pomaliza pa uthenga wake wabwino? Yohane 21:25 . . .

2. Ndi mayina ena ati amene Yesu amatchulidwa mu buku la Mateyu?

a. Mateyu 1:21

b. Mateyu 1:23

c. Mateyu 3:17

d. Mateyu 12:8

e. Mateyu 16:16

f. Mateyu 19:16

3. Kodi Yesu amatchedwa yani mu mabuku limene likuyenderana ndi Bailo?

a. Marko 5:6-7

b. Luka 5:5

c. Yohane 1:35-36

d. John 1:49

e. 1 Akolinto 1:6-7

Josephus (Joh-SEE-fus), Wodziwa za mbiri wa chi Yuda amene anabadwa mu chaka cha A.D. 37 amene anali wosakhulupirira , analemba zoona za kupachikidwa kwa Yesu. Ngakhale kuti Josephus samakhulupirira kuti Yesu ndi Mesiya, analemba izi zokhudzana ndi Yesu:

“Tsopano, panali munthu uyu wa nzeru , ngati nkoyenera kumutcha munthu, poti anali wochita ntchito za bwino, mpunzitsi wa anthu wa choonadi. Anakopa Ayuda ngakhale a Mitundu. Anali Khristu, ndipo pamene Pilato pa kukhumba kwa anthu akuluakulu mwa ife, analamula apachikidwe pa mtanda, iwo anankonda Iye poyamba sanantaye; poti anaonekeranso kwa iwo wamoyo pa tsiku la chitatu, monga momwe aneneri a uzimu analoserandi zikwi khumi za zinthu zodabwitsa zokhudza Iye. Ndipo mtundu wa Akhristu wotchedwa chifukwa cha Iye ukanalipo osatha mpaka lero.”

—Antiquities

Ma uneneri ochepa okhudza Mesiya

Uneneri

Kukwaniritsidwa

Adzabadwa mwa namwali. Kubadwa mwa namwali Yesu

Yesaya 7:14 (742B.C.)
Chifukwa chache Ambuye mwini yekha
adzakupatsani chizindikiro, taonani namwali
adzaima, nadzabala mwana wa mwamuna,
nadzamucha dzina lache Imanueli. (NASB)


Mateyu 1:22-23
Ndipo zonsezi zinakhala kuti chikachitidwe chonenedwa ndi Ambuye mwa mneneri, ndi kuti, Onani namwali adzaima, nadzabala mwana wa mwamuna dzina lace, Emanueli;
(ndilosandulika, “Mulungu nafe”).

Malo ake obadwira

Kubadwa kwa Yesu mu Betelehem.

Micah 5:2 (710B.C.)
Ambuye akuti, “Betelehemu Efrata, ndiwe
wa ngono kuti ukhale mwa zikwi za Yuda, mwa iwe mudzatuluka wowereza mu Israyeli;
matulukiro ake ndiwo a kale lomwe, kuyambira nthawi yosayamba.

Mateyu 2:1a
Yesu adabadwa mu mzinda
wa Betelehemu wa Yudea mu nthawi imene Herodi adali mfumu.
Adzakanidwa ndi anthu Ache.

Yesu adakanidwa.

Isaiah 53:3 (712B.C.)
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wa zisoni, ndiwodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu ombisira anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamulemekeza.

Yohane 1:11
Anadza kwa zache za Iye yekha, koma dziko silidamuzindikira Iye.
Adzaperekedwa ndi bwenzi Yesu adaperekedwa ndi m'modzi mwa ophunzira.
Salimo 41:9 (1062B.C.)
Ngakhale bwenzi langa leni leni, amene
ndamkhulupirira, ndiye amene anadyako mkate wanga, adandikwezera chidendene chache.
Marko 14:10
Ndipo Yudase Iskariote, ndiye mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anachoka napita kwa ansembe akulu, kuti akampereke Iye kwa iwo.
Adzauka kwa akufa. Yesu anauka patatha masiku atatu m'manda.
Salimo 16:10 (1040 B.C.)
…akuti simudzasiya moyo wanga kumanda;
simudzalora okondedwa wanu avunde.


Mateyu 28:5-6
Koma ngelo anayankha nati kwa akaziwo,
"Musaope inu; pakuti ndidziwa inu muli kufuna Yesu, amene anapachikidwa. Iye mulibe muno iai; pakuti anauka, monga ananena .idzani muno mudzaone malo omwe anagonamo Ambuye.”



4. Ziganizo zili mmusimu zikukamba za mbiri za Yesu. Onani pa mafunso oti
muyankhe, ndi zofananiza malemba a chiganizo ndi mau oyenerera mbaibulo:

a. Makolo Ake .......................b. Ubatizo Wake .....................c. Wake choyamba chake


Mateyu 1:1-17. . . . .

Yohane 2:1-11. . . . .


Marko 1:9-11 . . . . .

“Khristu ndi fanizo la Mulungu wosaonekayo..."
—Akolose 1:15

Pemphero Lotseka

Zikomo Ambuye Mulungu. Taphunzira za mbiri za Yesu mu phunziro ili. Tiphunzitseni za mbiri pamene tikupitiliza maphunziro awa. Tithanndizeni kupeza nthawi yowerenga phunziro ya sabata ya mawa. Tapemphera mu dzina la Yesu, ame.

 

 
 

 

YESU NDI NDANI?

 
 
Copyright ©  2023 www.UnitedCaribbean.com. All rights reserved. Disclaimer Click to Contact us