Project Hope     home >>stonecroft>> yesu ndani? >>phunziro 4 >>phunziro 5
Stonecroft - YESU NDI NDANI?- Phunziro #5
Women's Empowerment Program
Sports Bible Club
Living Water Bible Club

Yesu alikuti tsopano?

Pemphero

Mulungu wa mpamvu, tsekulani maso athu ndi makuti athu pamene tiwerenga tonse limodzi. Zimene tikuwerenga m'mau anu ndi zofunika kwambiri. mutikuze ife, Ambuye.
Tithandizeni tikule mukumvetsetsa kwa chimene inu uli. Tapemphera mu dzina la Yesu, Ame.


Kuwerenga Baibulo kwa Sabata:

Werengani gawo pansipa ndipo lembani kuyi ganizo kuti Yesu alikuti lero.

Machitidwe 1:6-11

Machitidwe 2:32-35

Aheberi 4:14-16

Agalatia 2:15-20

Aefeso 3:14-21

Akolose 1:27-29

1 Petulo 3:22


1. Luka analemba za zimene zidzachitike iye akauka. Werengani Machitidwe 1:1-11, dzalani mu magawo awa ndi mawu awa. . . . .

wamoyo kumbuyo 40 atumwi
mtambo kumwamba kulankhula zoyera
Yesu

Kwa masiku ........... atauka kwa akufa, Yesu anaonekera kwa......................nthawi za
mbiri ndi mjira zosiyana kuonetsera kuti anali ndi ........................... Anamuona Iye ndipo
analankhula naye. Iye ........................ iwo za zinthu zimene zidzachitika.

Tsiku lina, pamene Yesu analankhula nawo, anakwera ku ........................... akumuona.
......................... unamubisa. Anthu awiri ovala zoyera anawauza ................, amene watengedwa .............................., ........................... imnene amuonera akukwera ku mwamba.


2. Baibulo linalemba mowirikiza kuti Yesu anaonekera kwa anthu atauka kwa
akufa. Werengani ma gawo a Baibulo alipansiwa ndipo mulembe kwa iwo amene
Yesu aanawaonekera..

a. Yohane 20:14-18

b. Luka 24:13-15

c. Johane 20:26-29

d. 1 Akolinto 15:5

e. Yohane 21:1

f. 1 Akolinto 15:6

g. 1 Akolinto 15:7

3. Yesu alikuti lero? Aheberi 12:2

4. Yesu akutichitira chani lero? Aheberi 7:24-25

5. Kodi imfa ya Yesu inapindula chani kwa ife? Aroman 5:8-9

6. Yesu anafa pa mtanda ndi kuukanso kuti tikakhululukidwe ndi kukhala pa ubale
ndi Iye. Tikuyenera kumfusa Yesu atikhululukire ndi kumuitana kulowa m'moyo
mwathu. Ichi ndi chinthu chimene tikuyenera kuchita pa tokha. Palibe angatichitire
ichi. Ngati simukukumbukira nthawi imene munamuitana Yesu kulowa mu mtima
mwanu mutha kumuitana pompano.

Kuika chikhulupiriro chanu mwa Yesu ndi kulandira chikhululukiro ndi mphatso ya moyo wosatha.—

a. Zindikirani Yesu anakulengani inu kuti mukakhale pa chiyanjano ndi Iye. Amakukoni ndipo amafuna inu mumkonde ndi zanu zonse.

b. Zindikirani ndinu ochimwa. Simungadzipulumutse nokha.

c. Khulupirirani Yesu anafa pa mtanda kupereka dipo la tchimo lanu, kuti anauka kwa akufa, ndipo kuti ali wamoyo lero. Khulupirirani izi mu mtima mwanu osati mu mutu mwanu mokha.

d. Lankhulani ndi Mulungu m'moyo mwanu:
1) Funsani Yesu alowe m'moyo mwanu.
2) Bvomerezani ndipo mulape machimo anu, zimene zitanthauza kubwerera ku
machimo anu ndi kutembenukira kwa Mulungu.
3) Mufunseni akhululukire machimo anu.
4) Perekani moyo wanu kwa Yesu. Mloleni akhale mbuye wanu.

e. Uzani ena zimene mwachita.

f. Uzani gulu lanu la za chisankho chanu chimene mwapanga.

g. Ngati mwalandira Yesu Christu ngati mpulumutsi, lembani tsiku. Ndi tsiku loti
mudzilikumbukira! Ngati munamulandira pa kale, lembani tsiku limene
munamulandirira (perekani tsiku longoganizira kapena zaka ngati simuli
otsimikizika za nthawi imene munamulandira Yesu)

7.Kodi ma vesi awa amavumbulutsa chani pa za iwo amene afunsa Yesu Khristu
kuti alowe mu mtima mwawo.

a. Agalatiya 2:20

b. 1 Akorinto 3:16-17
1 Akorinto 6:19

c. Aroma 8:9-11

8. Berezani vesi loloweza imene mwapatsidwa polemba mau obisika m'mene muli
mipata pansipa:

Machitidwe 4:.......
Ndipo palibe ............................ mwa wina yense, pakuti palibe ................. lina pansi pa thambo la ............................, lopatsidwa mwa .................., limene tiyenera kupulumutsidwanalo.

9. Yamikani Ambuye pakukuwonetserani m'mene mungakhalire pa ubale ndi Iye.
Mufunseni adziwonetsere Yekha m'moyo wanu. Onjezerani maganizo anu ndipo
lembani pemphero lanu apa.

Pemphero Lotsekera

Wokondedwa Mbuye Yesu, taphunzira za mbiri za inu. Zikomo chifukwa cha Mzimu wanu
Woyera, amene munamutumiza kudzatiphunzitsa ndi kutitsogolera. Tiphunzitseni njira
zimene tingaphunzitsirrire wena zimene taphunzira. Tiphunzitseni pamene tikuwerenga
phunziro lomaliza. Tapemphera mu dzina la Lanu, ame.

 
 

 

YESU NDI NDANI?

 
 
Copyright ©  2023 www.UnitedCaribbean.com. All rights reserved. Disclaimer Click to Contact us