|  
               
               Stonecroft Stonecroft Training Mndandanda wa Utatu Malangizo Otsogolera Mavesi a m'BaibuloAdult Stonecroft International The International Team  English YDT Teachings Maphunziro a AnaMalawi Moringa Projects    |  | home >>stonecroft>>mzimu 
            woyera uli kuti?>> mavesi a m'baibulo  >>  phunziro 1  >>  phunziro 2
             
            
             
           KODO MZIMU WOVERA ULI KUTI?   - Mavesi a m'Baibulo - Phunziro  #2 
 
 Kuwerenga Baibulo mlungu ndi mlungu Yohane 3: 1-131Koma panali munthu wa Afarisi, dzina lace Nikodemo, mkulu wa Ayuda,2Iyeyu 
              anadza kwa Yesu usiku, nati kwa iye, Rabi, tidziwa kuti Inu ndinu 
              mphunzitsi wocokera kwa Mulungu; pakuti palibe munthu akhoza kucita 
              zizindikilo zimene inu mucita, ngati Mulungu sakhala naye, 3Yesu 
              anayankha nati kwa iye, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu 
              sabadwa mwatsopano, sakhoza kuona Ufumu wa Mulungu. 4Nikodemoananena 
              kwa iye, Munthu akhoza bwanji kubadwa atakalamba? Kodi akhoza kulowanso 
              m'mimba ya amace ndi kubadwa? 5Yesu anayankha, Indetu, indetu, ndinena 
              ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu, sakhoza kulowa 
              ufumu wa Mulungu. 6Cobadwa m'thupi cikhala thupi, ndipo cobadwa 
              mwa Mzimu, cikhala mzimu. 7Usadabwe cifukwa ndinati kwa iwe, Uyenera 
              kubadwa mwatsopano. 8Mphepo iomba pomwe ifuna, ndipo ukumva mau 
              ace, komavsudziwa, kumene icokera, ndi kumene imuka; cotero ali 
              yense wobadwa mwa Mzimu. 9Nikodemo anayankha nati kwa iye, Izi zingatheke 
              bwanji? 10Yesu anayankha nati kwa iye, Kodi uli mphunzitsi wa Israyeli, 
              ndipo sudziwa izi? 11Indetu, indetu, ndinena kwa iwe, Tilankhula 
              cimene ticidziwa, ndipo ticita umboni za cimene taeiona; ndipo umboni 
              wathu simuulandira. 12Ngati ndakuuzani za pansi pano, ndipo simukhulupira, 
              mudzakhulupira bwanji, ngati ndikuuzani za Kumwamba? 13Ndipo kulibe 
              munthu anakwera Kumwamba, koma iye wotsikayo kucokera Kumwamba, 
              ndiye Mwana wa munthu, wokhala m'Mwambayo.
 Yohane 3: 14-2114Ndipo monga Mose anakweza njoka m'cipululu, cotero Mwana wa munthu 
              ayenera kukwezedwa;15kuti yense wakukhulupira akhale nao moyo wosatha 
              mwa iye.
 16Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana 
              wace wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira iye asatayike, koma 
              akhale nao moyo wosatha. 17Pakuti Mulungu sanatuma Mwana wace ku 
              dziko lapansi, kuti akaweruze dziko lapansi, koma kuti dziko lapansi 
              likapulumutsidwe ndi iye.18Wokhulupirira Iye saweruzidwa; wosakhulupira 
              waweruzidwa ngakhale tsopano, cifukwa sanakhulupirira dzina la Mwana 
              wobadwa yekha wa Mulungu.19Koma ciweruziro ndi ici, kuti kuunika 
              kunadza ku dziko lapansi, ndipo anthu anakonda mdima koposa kuunika; 
              pakuti nchito zao zinali zoipa. 20Pakuti yense wakucita zoipa adana 
              nako kuunika, ndipo sakudza kwa kuunika, kuti zingatsutsidwe nchito 
              zace.
 21Koma wocita coonadi adza kukuunika, kuti nchito zace zionekere 
              kuti zinacitidwa mwa Mulungu. Macitidwe 1: 1-111TAONANI Teofilo inu, mau aja oyamba ndinakonza, za zonse Yesu anayamba 
              kuzicita ndi kuziphunzitsa, 2kufikira tsiku lija anatengedwa kunka 
              Kumwamba, atatha kulamulira mwa Mzimu Woyera atumwi amene adawasankha; 
              3kwa iwonso anadzionetsera yekha wamoyo ndi zitsimikizo zambiri, 
              zitatha zowawa zace, naonekera kwa iwo masiku makumi anai, ndi kunena 
              zinthu za Ufumuwa Mulungu; 4ndipo e posonkhana nao pamodzi, anawalamulira 
              asacoke ku Yerusalemu, komatu alindire lonjezano la Atate, limene, 
              anati, munalimva kwa Ine; 5pakuti Yohane anabatizadi ndi madzi; 
              koma inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera, asanapite masiku ambiri.
 6Pamenepo iwowa, atasonkhana pamodzi, anamfunsa iye, nanena, Ambuye, 
              kodi nthawi yino mubwezera ufumu kwa Israyeli? 7Koma anati kwa iwo, 
              Sikuli kwa inu kudziwa nthawi kapena nyengo, zimene Atate anaziika 
              m'ulamuliro wace wa iye yekha. 8Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu 
              Woyera atadza pa inu: ndipo mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, 
              ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, ndi kufikira malekezero ace 
              a dziko. 9Ndipo m'mene adanena izi, ali cipenyerere iwo, ananyamulidwa; 
              ndipo mtambo unamlandira iye kumcotsa kumaso kwao. 10Ndipo pakukhala 
              iwo cipenyerere kumwamba pomuka iye, taonani, amuna awiri obvala 
              zoyera anaimirira pambali pao; 11amenenso anati, Amuna a ku Galileya, 
              muimiranji ndi kuyang'ana kumwamba? Yesu amene walandiridwa kunka 
              Kumwamba kucokera kwa inu, adzadza momwemo monga munamuona alinkupita 
              Kumwamba. Macitidwe 2: 1-131Ndipo pakufika tsiku la Penteskoste, anali onse pamodzi pa malo 
              amodzi.2Ndipo mwadzidzidzi anamveka mau ocokera Kumwamba ngati mkokomo 
              wa mphepo yolimba, nadzaza nyumba yonse imene analikukhalamo. 3Ndipo 
              anaonekera kwa iwo malilime ogawanikana, onga amoto; ndipo unakhala 
              pa iwo onse wayekha wayekha. 4Ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, 
              nayamba kulankhula ndi malilime ena, monga Mzimu anawalankhulitsa.
 5Koma anali m'Yerusalemu okhalako Ayuda, amuna opembedza, ocokera 
              ku mtundu uli wonse pansi pa thambo. 6Koma pocitika mau awa, unyinji 
              wa anthu unasonkhana, nusokonezedwa, popeza yense anawamva alikulankhula 
              m'cilankhulidwe cace ca iye yekha. 7Ndipo anadabwa onse, nazizwa, 
              nanena, Taonani, awa onse alankhulawa sali Agalileya kodi? 8ndipo 
              nanga ife timva bwanji, yense m'cilankhulidwe cathu cimene tinabadwa 
              naco? 9Aparti ndi Amedi, ndi Aelami, ndi iwo akukhala m'Mesopotamiya, 
              m'Yudeya, ndiponso m'Kapadokiya, m'Ponto, ndi m'Asiya; 10m'Frugiya, 
              ndiponso m'Pamfuliya, m'Aigupto, ndi mbali za Libiya wa ku Kurene, 
              ndi alendo ocokera ku Roma, ndiwo Ayuda, ndiponso opinduka, 11Akrete, 
              ndi Aarabu, tiwamva iwo alikulankhula m'malilime athu zazikuru za 
              Mulungu. 12Ndipo anadabwa onse, nathedwa nzeru, nanena wina ndi 
              mnzace, Kodi ici nciani? 13koma ena anawaseka, nanena kuti, Akhuta 
              vinyo walero. Macitidwe 2: 14-2114Koma Petro, anaimirira pamodzi ndi khumi ndi mmodziwo, nakweza 
              mau ace, nanena kwa iwo, nati, Amuna inu Ayuda, ndi inu nonse akukhala 
              kwanu m'Yerusalemu, ici cizindikirike kwa inu, ndi po cherani khutu 
              mau anga. 15Pakuti awa sanaledzera monga muyesa inu; pakuti ndi 
              ora lacitatulokha la tsiku;16komatu ici ndi cimene cinanenedwa ndi 
              mneneri Yoeli, 17Ndipo kudzali m'masiku otsiriza, anena Mulungu, 
              Ndidzathira ca Mzimu wansa pa thupi liri lonse, Ndipo ana anu amuna, 
              ndi akazi adzanenera, Ndipo anyamata anu adzaona masomphenya, Ndi 
              akulu anu adzalota maloto; 18Ndiponso pa akapolo anga ndi pa adzakazi 
              anga m'masiku awa Ndidzathira ca Mzimu wanga; ndipo adzanenera.
 
 19Ndipo ndidzapatsa zodabwitsa m'thambo la kumwamba, Ndi zizindikilo 
              pa dziko lapansi; Mwazi, ndi moto, ndi mpweya wautsi; 20Dzuwa lidzasanduka 
              mdima, Ndi mweziudzasanduka mwazi, Lisanadze tsiku la Ambuye, Lalikuru 
              ndi loonekera; 21Ndipo kudzali, kuti yense amene akaitana pa dzina 
              la Ambuye adzapulumutsidwa. Macitidwe 2: 36-4236Pamenepo lizindikiritse ndithu banja liri lonse la Israyeli, kuti 
              Mulungu anamuyesa Ambuye ndi Kristu, Yesu amene inu munampacika.
 37Koma pamene anamva ici, analaswa mtima, natitu kwa Petro ndi 
              atumwi enawo, Tidzacita ciani, amuna inu, abale? 38Koma Petro anati 
              kwa iwo, Lapani, batizidwani yense wa inu m'dzina la Yesu Kristu 
              kuloza ku cikhululukiro ca macimo anu; ndipo mudzalandira mphatso 
              ya Mzimu Woyera. 39Pakuti lonjezano 1 liri kwa inu, ndi kwa ana 
              anu, 2 ndi kwa onse akutali, 3 onse amene Ambuye Mulungu wathu adzaitana. 
              40Ndipo ndi mau ena ambiri anacita umboni, nawadandaulira iwo, nanena, 
              Mudzipulumutse kwa mbadwo uno wokhotakhota.41Pamenepo iwo amene 
              analandira mau ace anabatizidwa; ndipo anaonjezedwa tsiku lomwelo 
              anthu ngati zikwi zitatu. 42Ndipo 4 anali cikhalire m'ciphunzitso 
              ca atumwi ndi m'ciyanjano, m'kunyema mkate ndi mapemphero. Aroma 8:16 16Mzimu yekha acita umboni pamodzi ndi mzimu wathu, kuti tiri ana 
              a Mulungu;
 Mzimu wa Mulungu mu Chipangano Chakale 1. Genesis 1: 22Dziko lapansi ndipo linali lopanda kanthu; ndipo mdima unali pamwamba 
              pa nyanja; ndipo mzimu wa Mulungu unaliokufungatira pamwamba pa 
              madzi.
 Yesaya 40: 12-1412Ndani wayesa madzi m'dzanja lace, nayesa thambo ndi cikhato, ndi 
              kudzaza pfumbi la nthaka m'nsengwa, ndi kuyesa mapiri m'mbale zoyesera, 
              ndi zitunda m'mulingo?
 13Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lace, 
              ndi kumphunzitsa Iye? 14Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza 
              Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya ciweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru 
              ndi kumuonetsa njira ya luntha?
 2. a. Yobu 33: 44Mzimu wa Mulungu unandilenga, Ndi mpweya wa Wamphamvuyonse umandipatsa 
              moyo.
  b. Ezekieli 36:2727Ndipo ndidzaika mzimu wanga m'kati mwanu, ndi kukuyendetsani m'malemba 
              anga; ndipo mudzasunga maweruzo anga ndi kuwacita.
  c. Mika 3: 88Koma ine ndidzala nayo mphamvu mwa Mzimu ya Yehova, ndi ciweruzo, 
              ndi camuna, kufotokozera Yakobo kulakwa kwace, ndi kwa Israyeli 
              cimo lace.
  d. 2 Samueli 23: 22Mzimu wa Yehova unalankhula mwa ine, Ndi mau ace anali pa lilime 
              langa,
  Yesaya 11: 22ndipo mzimu wa Yehova udzambalira iye mzimu wanzeru ndi wakuzindikira, 
              mzimu wa uphungu ndi mphamvu, mzimu wakudziwa ndi wakuopa Yehova;
 Eksodo 31 :33ndipo ndamdzaza nd mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi cidziwitso, 
              ndi m'nchito ziri zonse,
 Masalmo 51:1111Musanditaye kundicotsa pamaso panu; Musandicotsere Mzimu wanu 
              Woyera.
 Mzimu Woyera mu chipangano chatsopano Yohane 14:1616Ndipo Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe 
              yina, kuti akhale ndi inu ku nthawi yonse,
 Mzimu Woyera mu moyo wa Khristu 3. Luka 4: 16-1816Ndipo anadza ku Nazarete, kumene analeredwa; ndipo tsiku la Sabata 
              analowa m'sunagoge, monga anazolowera, naimiriramo kuwerenga m'kalata.17Ndipo 
              anapereka kwa iye buku la Yesaya mneneri. Ndipo m'mene iye adafunyulula 
              bukulo, anapeza pomwe panalembedwa, 18Mzimu wa Ambuye uli paine, 
              Cifukwa cace iye anandidzoza Ine ndiuze anthu osauka Uthenga Wabwino: 
              Anandituma Ine kulalikira am'nsinga mamasulidwe, Ndi akhungu kuti 
              apenyenso, Kuturutsa ndi ufuru ophwanyika,
  Luka 4: 11Ndipo Yesu, wodzala ndi Mzimu Woyera, anabwera kucokera ku Yordano, 
              natsogozedwa ndi Mzimu kunka kucipululu kukayesedwa ndi mdierekezi 
              masiku makumi anai.
  Aroma 8:1111Koma ngati Mzimu wa iye amene adaukitsa Yesu kwa akufa akhalabe 
              mwa inu, iye amene adaukitsa Kristu Yesu kwa akufa adzapatsanso 
              moyo matupi anu akufa, mwa Mzimu wace wakukhala mwa inu.
 
 Macitidwe 1: 1-2
 1TAONANI Teofilo inu, mau aja oyamba ndinakonza, za zonse Yesu anayamba 
              kuzicita ndi kuziphunzitsa, 2kufikira tsiku lija anatengedwa kunka 
              Kumwamba, atatha kulamulira mwa Mzimu Woyera atumwi amene adawasankha;
  Mateyu 1: 18-2018Ndipo kubadwa kwace kwa Yesu Kristu kunali kotere: Amai wace Mariya 
              anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanakomane iwowo, anapezedwa 
              iye ali ndi pakati mwa Mzimu Woyera. 19Koma Yosefe, mwamuna wace, 
              anali wolungama, ndiponso sanafuna kunyazitsa iye, nayesa m'mtima 
              kumleka iye m'tseri, 20Koma pakusinkhasinkha iye zinthu izi, onani, 
              mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye m'kulota, nanena, Yosefe, mwana 
              wa Davide, usaope kudzitengera wekha Mariya mkazi wako; pakuti ico 
              colandiridwa mwa iye ciri ca Mzimu Woyera.
 Ntchito Mzimu Woyera 'm mu kulemba Baibulo  4. 2 Petro 1 : 2121pakuti kale lonse cinenero sicinadza ndi cifuniro ca munthu; koma 
              anthu a Mulungu, ogwidwa ndi Mzimu Woyera, analankhula.
 1 Akorinto 2:1313Zimenenso tilankhula, si ndi mau ophunzitsidwa ndi nzeru za munthu, 
              koma ophunzitsidwa ndi Mzimu; ndi kulinganiza zamzimu ndi zamzimu.
 Mzimu Woyera mu miyoyo yathu   Agalatiya 3:2727Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Kristu mudabvala Kristu.
  Aroma 8:1515Pakuti inu simunalandira mzimu wa ukapolo kucitanso mantha; koma 
              munalandira mzimu waumwana, umene tipfuula nao, kuti, Abba, Atate,
 
 2 Akorinto 3:18
 18Koma ife tonse ndi nkhope yosaphimbika popenyerera monga mwa kalirole 
              ulemerero wa Ambuye, tisandulika m'cithunzihunzi comweci kucokera 
              kuulenerero kumka kuulemerero, monga ngati kucokera kwa Ambuye Mzimu.
  1 Akorinto 3: 16-1716Kodi simudziwa kuti muli Kacisi wa Mulungu, ndi kuti Mzimu wa 
              Mulungu agonera mwa inu? 17Ngati wina aononga kacisi wa Mulungu, 
              ameneyo Mulungu adzamuononga; pakuti kacisi wa Mulungu ali wopatulika, 
              ameneyo ndi inu.
  Yohane 6:6323koma zinacokera ngalawa zina ku Tiberiya, pafupi pa malo pomwe 
              adadyapo mkate m'mene Yesu adayamika;
 
 |  |