|  
               
               Stonecroft Stonecroft Training Mndandanda wa Utatu Malangizo Otsogolera Mavesi a m'BaibuloAdult Stonecroft International The International Team  English YDT Teachings Maphunziro a AnaMalawi Moringa Projects    |  | home >>stonecroft>>mzimu 
            woyera uli kuti?>> mavesi a m'baibulo  >>  phunziro 3 >>  phunziro 4             
            
             
KODO MZIMU WOVERA ULI KUTI?   - Mavesi a m'Baibulo - Phunziro  #4 
 
 Kuwerenga Baibulo mlungu ndi mlungu 1 Akorinto 13: 1-131Ndingakhale ndilankhula malilime a anthu, ndi a angelo, koma ndiribe 
              cikondi, ndikhala mkuwa woomba, kapena nguli yolira. 2Ndipo ndingakhale 
              ndikhoza kunenera, ndipo ndingadziwe zinsinsi zonse, ndi nzeru zonse, 
              ndipo ndingakhale ndiri naco cikhulupiriro conse, kuti ndikasendeza 
              mapiri, koma ndiribe cikondi, ndiri cabe. 3Ndipo ndingakhale ndipereka 
              cuma cangaconsekudyetsa osauka, ndipo ndingakhalendipereka thupi 
              langa alitenthe m'moto, koma ndiribe cikondi, sindipindula kanthu 
              ai. 4Cikondi cikhala cilezere, ciri cokoma mtima; cikondi sicidukidwa; 
              cikondi sicidziwa kudzitamanda, sicidzikuza, 5sicicita zosayenera, 
              sicitsata za mwini yekha, sicipsa mtima, sicilingirira zoipa; 6sicikondwera 
              ndi cinyengo, koma cikondwera ndi coonadi;7cikwirira zinthu zonse, 
              cfkhulupirira zinthu zonse, ciyembekeza zinthu zonse, cipirira zinthu 
              zonse. 8Cikondi sicitha nthawizonse, koma kapena zonenera zidzakhala 
              cabe, kapena malilime adzaleka, kapena nzeru idzakhala cabe.9Pakuti 
              ife tidziwa mderamdera, ndimo tinenera mderamdera. 10Koma pamene 
              cangwiro cafika, tsono camderamdera cidzakhalacabe. 11Pamene ndinali 
              mwana, ndinalankhula ngati mwana, ndinalingirira ngati mwana, ndinawerenga 
              ngati mwana; tsopano ndakhala munthu, ndayesa cabe zacibwana. 12Pakuti 
              tsopano tipenya m'kalirole, ngati cimbuuzi; koma R pomwepo maso 
              ndi maso. Tsopano ndizindikira mderamdera; koma pomwepo ndidzazindikiratu, 
              monganso ndazindikiridwa. 13Ndipo tsopano zitsala cikhulupiriro, 
              dyembekezo, cikondi, zitatu izi; koma cacikuru ca izi ndico cikondi.
 Aroma 8: 1-81Cifukwa cace tsopano iwo akukhala mwa Kristu Yesu alibe kutsutsidwa.2Pakuti 
              cilamulo ca mzimu wa moyo mwa Kristu Yesu candimasula ine ku lamulo 
              la ucimo ndi la imfa. 3Pakuti cimene cilamulo sicinathe kucita, 
              popeza cinafoka mwa thupi, Mulungu anatumiza Mwana wace wa iye yekha 
              m'cifanizo ca thupi la ucimo, ndi cifukwa ca ucimo, natsutsa ucimo 
              m'thupi; 4kuti coikika cace ca cilamulo cikakwaniridwe mwa ife, 
              amene sitiyendayenda monga mwa thupi, koma monga mwa mzimu. 5Pakuti 
              iwo amene ali monga mwa thupi asamalira zinthu za thupi; koma iwo 
              amene ali monga mwa mzimu, asamalira zinthu za mzimu: 6pakuti cisamaliro 
              ca thupi ciri imfa; koma cisamaliro ca mzimu ciri moyo ndi mtendere. 
              7Cifukwa cisamaliro ca thupi cidana ndi Mulungu; pakuti sicigonja 
              ku cilamulo ca Mulungu, pakuti sicikhoza kutero. 8Ndipo iwo amene 
              ali m'thupi sangathe kukondweretsa Mulungu.
 Aroma 8: 9-179Koma inu simuli m'thupi ai, koma mumzimu, ngatitu Mzimu wa Mulungu 
              akhalabe mwa inu. Koma ngati munthu alibe Mzimu wa Kristu, siali 
              wace wa Kristu. 10Ndipo ngati Kristu akhala mwa inu, thupilo ndithu 
              liri lakufa cifukwa ca ucimo; koma mzimu uli wamoyo cifukwa ca cilungamo. 
              11Koma ngati Mzimu wa iye amene adaukitsa Yesu kwa akufa akhalabe 
              mwa inu, iye amene adaukitsa Kristu Yesu kwa akufa adzapatsanso 
              moyo matupi anu akufa, mwa Mzimu wace wakukhala mwa inu.
 12Cifukwa cace, abale, ife tiri amangawa si ace a thupi ai, kukhala 
              ndi moyo monga mwa thupi; 13pakuti ngati mukhala ndi moyo monga 
              mwa thupi, mudzafa; koma ngati ndi mzimu mufetsa zocita zace za 
              thupi, mudzakhala ndi moyo.14Pakuti onse amene atsogozedwa ndi Mzimu 
              wa Mulungu, amenewo ali ana a Mulungu, 15Pakuti inu simunalandira 
              mzimu wa ukapolo kucitanso mantha; koma munalandira mzimu waumwana, 
              umene tipfuula nao, kuti, Abba, Atate, 16Mzimu yekha acita umboni 
              pamodzi ndi mzimu wathu, kuti tiri ana a Mulungu; 17ndipo ngati 
              ana, pomweponso olowa nyumba; inde olowa nyumba ace a Mulungu, ndi 
              olowa anzace a Kristu; ngatitu ife timva zowawa pamodzi naye, kuti 
              tikalaodirenso ulemerero pamodzi ndi iye. 1 Akorinto 12: 1-111Koma za mphatso zauzimu, abale, sindifuna kuti mukhale osadziwa.2Mudziwa 
              kuti pamene munali amitundu, munatengedwa kunka kwa mafano aja osalankhula, 
              monga munatsogozedwa. 3Cifukwa cace ndikuuzani inu, kuti palibe 
              munthu wakulankhula mwa Mzimu wa Mulungu, anena, Yesu ngwotembereredwa; 
              ndipo palibe wina akhoza kunena, Yew ali Ambuye, koma mwa Mzimu 
              Woyera.
 4Ndipo pali mphatso zosiyana, koma Mzimu yemweyo. 5Ndipo pali mautumiki 
              osiyana, koma Ambuye yemweyo. 6Ndipo pali macitidwe osiyana, koma 
              Mulungu yemweyo, wakucita zinthu zonse mwa onse. 7Koma kwa yense 
              kwapatsidwa maonekedwe a Mzimu kuti apindule nao. 8Pakuti kwa mmodzi 
              kwapatsidwa mwa Mzimu mau a nzeru; koma kwa mnzace mau a cidziwitso, 
              monga mwa Mzimu yemweyo: 9kwa wina cikhulupiriro, mwa Mzimu yemweyo; 
              ndi kwa wina mphatso za maciritso, mwa Mzimu mmodziyo; 10ndi kwa 
              wina macitidwe a mphamvu; ndi kwa wina cinenero; ndi kwa wina cizindikiro 
              ca mizimu; kwa wina malilime a mitundu mitundu; ndi kwa wina mamasulidwe 
              a malilime. 11Koma zonse izi acita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira 
              yense payekha monga afuna. 1 Yohane 4: 7-217Okondedwa, tikondane wins ndi mnzace: cifukwa kuti cikond cicokera 
              kwa Mulungu, ndipo yense amene akonda, abadwa kucokera kwa Mulungu, 
              namzindikira Mulungu, 8iye wosakonda sazindikira Mulungu; cifukwa 
              Mulungu ndiye cikondi. 9Umo cidaoneka cikondi ca Mulungu mwa ife, 
              kuti Mulungu anamtuma Mwana wace wobadwa yekha alowe m'dziko lapansi, 
              kuti tikhale ndi moyo mwa iye. 10Umo muli cikondi, sikuti ife tinakonda 
              Mulungu, koma kuti iye anatikonda ife, ndipo anatuma Mwana wace 
              akhale ciombolo cifukwa ca macime athu. 11Okondedwa, ngati Mulungu 
              anatikonda ife kotero, ffenso tiyenera kukondana wina ndi mnzaceo 
              12Palibe munthu adamuona Mulungu nthawi iri yonse; tikakondana wina 
              ndi mnzace, Mulungu akhala mwa ife, ndi cikondi cace cikhala cangwiro 
              mwa ife; 13m'menemo tizindikira kuti tikhala mwa iye, ndi iye mwa 
              ife, cifukwa anatipatsako Mzimu wace. 14Ndipo ife tapenyera, ndipo 
              ticita umboni kuti Atate anatuma Mwana akhale Mpulumutsi wa dziko 
              lapansi. 15Iye amene adzabvomereza kuti Yesu ali Mwana wa Mulungu, 
              Mulungu akhala mwa iye, ndi iye mwa Mulungu. 16Ndipo ife tazindikira, 
              ndipo takhulupirira cikondico Mulungu ali naco pa ife. Mulungu ndiye 
              cikondi, ndipo iye amene akhala m'cikondi akhala mwa Mulungu, ndipo 
              Mulungu akhala mwa iye. 17M'menemo cikondi cathu cikhala cangwiro 
              kuti tikhale nako kulimbika mtima m'tsiku la mlandu; citukwa monga 
              Iyeyuali, momwemo tiri ife m'dziko line lapansi.18Mulibe mantha 
              m'cikondi; koma cikondi cangwiro citaya kunja mantha, popeza mantha 
              ali naco cilango, ndipo wamanthayo sakhala wangwiro m'cikondi.19Tikonda 
              ife, cifukwa anayamba iye kutikonda. 20Munthu akati, kuti, Ndikonda 
              Mulungu, nadana naye mbale wace, ali wabodza: pakuti iye wosakonda 
              mbale ware amene wamuona, sakhoza kukonda Mulungu amene sanamuona. 
              21Ndipo lamulo ili tiri nalo locokera kwa iye, kuti iye amene akonda 
              Mulungu akondenso mbale wace.
 Galates 5: 16-2616Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse cilakolako 
              ca thupi. 17Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu 
              potsutsana nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna 
              musazicite. 18Ngati Mzimu akutsogolerani, simuli omvera lamulo. 
              19Ndipo nchito za thupi zionekera, ndizo dama, codetsa, kukhumba 
              zonyansa, kupembedza mafano, 20nyanga, madano, ndeu, kaduka, zopsa 
              mtima, zotetana, magawano, mipatuko, njiru, 21kuledzera, mcezo, 
              ndi zina zotere; zimene ndikucenjezani nazo, monga ndacita, kuti 
              iwo akucitacita zotere sadzalowa Ufumu wa Mulungu. 22Koma cipatso 
              ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza mtima, cifundo, 
              kukoma mtima, icikhulupirtro, 23cifatso, ciletso; pokana zimenezi 
              palibe lamulo. 24Koma iwo a Kristu Yesu adapacika thupi, ndi zokhumba 
              zace, ndi zilakolako zace.
 251 N gati tiri ndi moyo ndi Mzimu, ndi Mzimunso tiyende. 262 Tisakhale 
              odzikuza, outsana, akucitirana njiru. 1 Petro 5: 14b Mtendere ukhale ndi inu nonse muli mwa Kristu.
 1 Yohane 1: 99Ngati tibvomereza macimo athu, ali wokhulupirika ndi wolungama 
              iye, kuti atikhululukire macimo athu, ndi kutisambitsa kuticotsera 
              cosalungama ciri conse
  1. Agalatiya 5: 22-2322Koma cipatso ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza 
              mtima, cifundo, kukoma mtima, icikhulupirtro, 23cifatso, ciletso; 
              pokana zimenezi palibe lamulo.
 1 Akorinto 13:1313Ndipo tsopano zitsala cikhulupiriro, dyembekezo, cikondi, zitatu 
              izi; koma cacikuru ca izi ndico cikondi.
 Chipatso cha Mzimu  2. Mateyu 22: 34-4034Koma Afarisi, pakumva kuti Iye anatontholetsa Asaduki, anasonkhana.35Ndipo 
              mmodzi wa iwo, mphunzitsi wa cilamulo, anamfunsa ndi kumuyesa Iye, 
              nati, 36Mphunzitsi, lamulo lalikuru ndi liti la m'cilamulo? 37Ndipo 
              Yesu anati kwa iye, Uzikonda Ambuye Mulungu wako ndi mtima wako 
              wonse, ndi moyo wako wonse, ndi nzeru zako zonse. 38Ili ndilo lamulo 
              lalikuru ndi loyamba. 39Ndipo laciwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda 
              mnzako monga udzikonda iwe mwini. 40Pa malamulo awa awiri mpokolowekapo 
              cilamulo conse ndi aneneri.
  Kukonda 3. a. Akolose 3:1919Amuna inu, kondani akazi anu, ndipo musawawire mtima iwo.
  b. Luka 6: 27-2827Koma ndinena kwa inu akumva, Kondanani nao adani anu; citirani 
              zabwino iwo akuda inu, 28dalitsani iwo akutemberera inu, pemphererani 
              iwo akucitira inu cipongwe.
  c. Tito 2: 3-43Momwemonso akazi okalamba akhale nao makhalidwe oyenera anthu oyera, 
              osadierekeza, osakodwa naco cikondi ca pavinyo, akuphunzitsa zokoma; 
              4kuti akalangize akazi ang one akonde amuna ao, akonde ana ao,
  d. Yohane 13: 34-3534Ndikupatsani inu lamulo latsopano, kuti mukondane wina ndi mnzace; 
              monga ndakonda Inu, kuti inunso mukondane wina ndi mnzace. 351 Mwa 
              ici adzazindikira onse kuti muli akuphunzira anga, ngati muli naco 
              cikondano wina ndi mnzace.
  e. Mateyu 22:3939Ndipo laciwiri lolingana nalo ndili, Uzikonda mnzako monga udzikonda 
              iwe mwini.
  f. Aefeso 5: 22ndipo yendani m'cikondi monganso Kristu anakukondani inu, nadzipereka 
              yekha m'malo mwathu, copereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale pfungo 
              lonunkhira bwino.
 
 Aroma 12: 9-10
 9Cikondano cikhale copanda cinyengo, Dana naco coipa; gwirizana 
              naco cabwino. 10M'cikondano ca anzanu wina ndi mnzace mukondane 
              ndi cikondi ceni ceni; mutsogolerane ndi kucitira wina mnzace ulemu;
 Aroma 5: 55ndipo ciyembekezo sicicititsa manyazi; cifukwa cikondi ca Mulungu 
              cinatsanulidwa m'mitima mwathu mwa Mzimu Woyera, amene wapatsidwa 
              kwa ife.
 Chimwemwe Afilipi 4: 44Kondwerani mwa Ambuye nthawi zonse: ndibwerezanso kutero, kondwerani.
 Mtendere Afilipi 4: 6-76Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, 
              pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu. 7Ndipo 
              mtendere wa Mulungu wakupambana cidziwitso conse, udzasunga mitima 
              yanu ndi maganizo anu mwa Kristu Yesu.
 Yohane 14:27274 Mtendere ndikusiyirani inu, mtendere wanga ndikupatsani; Ine 
              sindikupatsani inu monga dziko lapansi lipatsa. 5 Mtima wanu usabvutike, 
              kapena usacite mantha.
 Chipiriro 4. Aroma 15: 55Ndipo Mulungu wa cipiriro ndi wa citonthozo apatse inu kuti mukhale 
              ndi mtima umodzi wina ndi mnzace, monga mwa Kristu Yesu;
 Mtima 5. Akolose 3:1212Cifukwa cace bvalani, monga osankhika a Mulungu, oyera mtima ndi 
              okondedwa, mtima wacifundo, kukoma mtima, kudzicepetsa, cifatso, 
              kuleza mtima;
 Ubwino 6. Aefeso 2:1010Pakuti ife ndife cipango cace, olengedwa mwa Kristu Yesu, kucita 
              nchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo.
 Kukhulupirika Luka 16: 10-1210Iye amene akhulupirika m'cacing'onong'ono alinso wokhulupirika 
              m'cacikuru; ndipo iye amene ali wosalungama m'cacing'onong'ono alinso 
              wosalungama m'cacikuru. 11Cifukwa cace ngati simunakhala okhulupirika 
              m'cuma ca cosalungama, adzakhulupirira inu ndani ndi cuma coona? 
              12Ndipo ngati simunakhala okhulupirika ndi zace za wina, adzakupatsani 
              inu ndani za inu eni?
 7. 2 Atesalonika 3: 33Koma Ambuye ali wokhulupirika amene adzakukhazikitsani inu, nadzakudikirirani 
              kuletsa woipayo;
 Kudzichepetsa Afilipi 2: 3-83musacite kanthu monga mwa cotetana, kapena monga mwa ulemerero 
              wopanda pace, komatu ndi kudzicepetsa mtima, yense ayese anzace 
              omposa iye mwini; 4munthu yense asapenyerere zace za iye yekha, 
              koma yense apenyererenso za mnzaceo 5Mukhale nao mtima m'kati mwanu 
              umene unalinso mwa Kristu Yesu, 6ameneyo, pokhala nao maonekedwe 
              a Mulungu, sanaciyesa colanda kukhala wofana ndi Mulungu,7koma anadzikhuthula 
              yekha, natenga maonekedwe akapolo, nakhala m'mafanizidwe a anthu; 
              8ndipo popezedwa m'maonekedwe ngati munthu, anadzicepetsa yekha, 
              nakhala womvera kufikira imfa, ndiyo imfa ya pamtanda.
 Kudzigwira Tito 2: 11-1211Pakuti caonekera cisomo ca Mulungu cakupulumutsa anthu onse, 12ndi 
              kutiphunzitsa ife kuti, pokana cisapembedzo ndi zilakolako za dziko 
              lapansi, tikhale ndi moyo m'dziko lino odziletsa, ndi olungama, 
              ndi opembedza;
 Afilipi 1:1111odzala nacocipatso ca cilungamo cimene ciri mwa Yesu Kristu, kucitira 
              Mulungu ulemerero ndi ciyamiko.
 Mphatso za mzimu Agalatiya 5:22-2322Koma cipatso ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza 
              mtima, cifundo, kukoma mtima, icikhulupirtro, 23cifatso, ciletso; 
              pokana zimenezi palibe lamulo.
 1 Akorinto 12:1111Koma zonse izi acita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira yense payekha 
              monga afuna.
 1 Petro 4:1010monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo 
              okoma a cisomo ca mitundu mitundu ca Mulungu;
  8. 1 Petro 4:1010monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo 
              okoma a cisomo ca mitundu mitundu ca Mulungu;
 9. 1 Akorinto 12: 8-108Pakuti kwa mmodzi kwapatsidwa mwa Mzimu mau a nzeru; koma kwa mnzace 
              mau a cidziwitso, monga mwa Mzimu yemweyo: 9kwa wina cikhulupiriro, 
              mwa Mzimu yemweyo; ndi kwa wina mphatso za maciritso, mwa Mzimu 
              mmodziyo;
 Aroma 12: 6-86Ndipo pokhala ife ndi mphatso zosiyana, monga mwa cisomo copatsidwa 
              kwa ife, kapena mphatso yakunenera, tinenere monga mwa muyeso wa 
              cikhulupiriro;7kapenayakutumikira, tidzipereke ku utumiki uwu; kapena 
              iye wakuphunzitsa, kukuphunzitsako;
 1 Akorinto 12:1111Koma zonse izi acita Mzimu mmodzi yemweyo, nagawira yense payekha 
              monga afuna.
   |  |