|  
               
               Stonecroft Stonecroft Training Mndandanda wa Utatu Malangizo Otsogolera Mavesi a m'BaibuloAdult Stonecroft International The International Team  English YDT Teachings Maphunziro a AnaMalawi Moringa Projects    |  | home >>stonecroft>>mzimu 
            woyera uli kuti?>> mavesi a m'baibulo  >>  phunziro 2  >>  phunziro 3             
            
             
             KODO MZIMU WOVERA ULI KUTI?   - Mavesi a m'Baibulo - Phunziro  #3 
 
 Kuwerenga Baibulo mlungu ndi mlungu Yohane 14: 1-141Mtima wanu usabvutike; mukhulupirira Mulungu, khulupirirani Inenso.2M'nyumba 
              ya Atate wanga alimo malo okhalamo ambiri. Ngati sikudali kutero, 
              ndikadakuuzani inu; pakuti ndipita kukukonzerani inu malo. 3Ndipo 
              ngati ndipita kukakonzera inu malo, ndidzabweranso, ndipo ndidzalandira 
              inu kwa Ine ndekha; kuti kumene kuli Ineko, mukakhale inunso. 4Ndipo 
              kumene ndinkako Ine, mudziwa njira yace. 5Tomasi ananena ndi Iye, 
              Ambuye, sitidziwa kumene munkako; tidziwa njira bwanji? 6Yesu ananena 
              naye, ine ndinenjira, ndi coonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza 
              kwa Atate, koma mwa Ine.
 7Mukadazindikira ine mukadadziwa Atate wanganso; kuyambira tsopano 
              mumzindikira iye, ndipo mwamuona iye. 8Filipo ananena ndi iye, Ambuye, 
              tionetsereni ife Atate, ndipo citikwanira. 9Yesu ananena naye, Kodi 
              ndiri ndiinu nthawi yaikuru yotere, ndipo sunandizindikira, Filipo? 
              iye amene wandiona Ine waona Atate; unena iwe bwanji, Mutionetsere 
              Atate? 10Sukhulupirira kodi kuti ndiri Ine mwa Atate, ndi Atate 
              ali mwa Ine? Mau amene ndinena Ine kwa inu sindilankhula kwa Ine 
              ndekha; koma Atate wokhala mwa Ine acita nchito zace.11Khulupirirani 
              Ine, kuti Inendiri mwa Atate ndi Atate ali mwa Ine; koma ngati si 
              comweco, khulupirirani Ine cifukwa ca nchito zomwe. 12Indetu, indetu, 
              ndinena kwa inu, Wokhulupirira Ine, nchito zimene ndicita Ine adzazicitanso 
              iyeyu; ndipo adzacita zoposa izi; cifukwa ndipita Ine kwa Atate. 
              13Ndipo cimene ciri conse mukafunse m'dzina langa, ndidzacicita, 
              kuti Atate akalemekezedwe mwa Mwana.14Ngati mudzapempha kanthu m'dzina 
              langa, ndidzacita.  Yohane14: 15-3115Ngati mukonda Ine, sungani malamulo anga.
 16Ndipo Ine ndidzapempha Atate, ndipo adzakupatsani inu Nkhoswe 
              yina, kuti akhale ndi inu ku nthawi yonse, 17ndiye Mzimu wa coonadi; 
              amene dziko lapansi silingathe kumlandira, pakuti silimuona iye, 
              kapena kumzindikira iye. Inu mumzindikira iye; cifukwa akhala ndi 
              inu nadzakhala mwa inu. 18Sindidza-kusiyani inu mukhale ana amasiye; 
              ndidza kwa inu. 19Katsala kanthawi, ndipo dziko lapansi silindionanso 
              Ine; koma inu mundiona; popeza Ine ndiri ndi moyo inunso mudzakhala 
              ndi moyo. 20Tsiku lo mwelo mudzazindikira kuti ndiri Ine mwa Atate 
              wanga, ndi inu mwa Ine, ndi Ine mwa inu. 21Iye wakukhala nao malamulo 
              anga, ndi kuwasunga, iyeyu ndiye wondikonda Ine; koma wondikonda 
              Ine adzakondedwa ndi Atate wanga, ndipo line ndidzamkonda, ndipo 
              ndidzadzionetsandekha kwa iye.
 Yohane 15: 1-171Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam'munda. 2Nthambi 
              iri yonse ya mwa Ine yosabala cipatso, aicotsa; ndi iri y'onse yakubala 
              cipatso, aisadza, kuti ikabale cipatso cocuruka. 3Mwakhala okonzeka 
              tsopano inu cifukwa ca mau amene ndalankhula ndi inu, 4Khalani mwa 
              Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala cipatso pa 
              yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala 
              mwa Ine. 5Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zace: wakukhala mwa 
              Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala cipatso cambiri; pakuti kopanda 
              Ine simungathe kucita kanthu. 6Ngati wina sakhala mwa Ine, watayika 
              kunja monga nthambi, nafota; ndipo azisonkhanitsa nazitaya kumoto, 
              nazitentha. 7Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, 
              pemphani cimene ciri conse mucifuna ndipo cidzacitika kwa inu. 8Mwa 
              ici alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale cipatso cambiri; ndipo 
              mudzakhala akuphunzira anga. 9Monga momwe Atate wandikonda Ine, 
              Inenso ndakonda inu; khalani m'cikondi canga. 10Ngati musunga malamulo 
              anga mudzakhala m'cikondi canga; monga Ine ndasunga malamulo a Atate 
              wanga, ndipo ndikhala m'cikondi cace. 11Izi ndalankhula ndi inu, 
              kuti cimwemwe canga cikhale mwa inu, ndi kuti cimwemwe canu cidzale. 
              12Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzace, monga ndakonda 
              inu. 13Palibe munthu ali naco cikondi coposa ici, cakuti munthu 
              ataya moyo wace cifukwa ca abwenzi ace. 14Muli abwenzianga inu, 
              ngati muzicita zimene ndikulamulirani inu.
 15Sindichanso inu akapolo; cifukwa kapolo sadziwa cimene mbuye 
              wace acita; koma ndacha inu abwenzi; cifukwa zonse zimene ndazimva 
              kwa Atate wanga ndakudziwitsani. 16Inu simunandisankha Ine, koma 
              Ine ndinakusankhani inu, ndipo ndinakuikani, kuti mukamuke inu ndi 
              kubala cipatso, ndi kuti cipatso canu cikhale; kuti cimene ciri 
              conse mukapempha Atate m'dzina langa akakupatseni inu. 17Zinthu 
              izi ndilamulira inu, kuti mukondane wina ndi mnzace. Yohane 15: 18-2718Ngati dziko lapansi lida inu, mudziwa kuti lidada Ine lisanayambe 
              kuda inu.19Mukadakhala a dziko lapansi, dziko lapansi likadakonda 
              zace za lokha; koma popeza simuli a dziko lapansi, koma Ine ndinakusankhani 
              inu mwa dziko lapansi, cifukwa ca ici likudani inu. 20Kumbukilani 
              mau amene Ine ndinanena kwa inu, Kapolo sali wamkuru ndi mbuye wace. 
              Ngati anandilondalonda Ine, adzakulonda-londani inunso; ngati anasunga 
              mau anga, adzasunga anunso.21Koma izi zonse adzakucitirani cifukwa 
              ca dzina langa, cifukwa sadziwa wondituma Ine. 22Sindikadadza ndi 
              kulankhula nao sakadakhala nalo cimo; koma tsopano alibe cowiringula 
              pa macimo ao. 23Iye wondida Ine, adanso Atate wanga. 24Sindikadacita 
              mwa iwo nchito zosacita wina, sakadakhala nalo cimo; koma tsopano 
              anaona, nada: Ine ndi Atate wanganso, 25Koma citero, kuti mau olembedwa 
              m'cilamulo cao akwaniridwe, kuti, Anandida Ine kopanda cifukwa.
 26Koma pamene wafika Nkhoswe, amene Ine ndidzamtuma kwa inu kucokera 
              kwa Atate, ndiye Mzimu wa coonadi, amene aturuka kwa Atate, Iyeyu 
              adzandicitira Ine umboni. 27Ndipo inunso mucita umboni, pakuti muli 
              ndi Ine kuyambira ciyambi. Yohane 16: 1-151Izi ndalankhula ndi inu kuti mungakhumudwitsidwe. 2Adzakuturutsani 
              m'masunagoge; koma ikudza nthawi imene yense wakupha inu adzayesa 
              kuti atumikira Mulungu, 3Ndipo izi adzacita, cifukwa sanadziwa Atate, 
              kapena Ine.4Koma zinthu izi ndalankhula ndi inu kuti ikadza nthawi 
              yao, mukakumbukire kuti ndinakuuzani. Koma izi sindinanena kwa inu 
              kuyambira paciyambi, cifukwa ndinali pamodzi ndi inu. 5Koma tsopano 
              ndimuka kwa iye wondituma Ine; ndipo palibe wina mwa inu andifunsa 
              Ine, Munka kuti? 6Koma cifukwa ndalankhula izi ndi inu cisoni cadzala 
              mumtima mwanu.
 7Koma ndinena Ine coonadi ndi inu; kuyenera kwa inu kuti ndicoke 
              Ine; pakuti ngati sindicoka, Nkhosweyo sadzadza kwa inu; koma ngati 
              ndipita ndidzamtuma iye kwa inu. 8Ndipo atadza Iyeyo, adzatsutsa 
              dziko lapansi za macimo, ndi za cilungamo, ndi za ciweruziro; 9za 
              macimo, cifukwa sakhulupirira Ine; 10za cilungamo, cifukwa ndinka 
              kwa Atate, ndipo simundionanso; 11za ciweruziro, cifukwa mkuru wa 
              dziko ili lapansi waweruzidwa. 12Ndiri nazo zambirinso zakunena 
              kwa inu, koma simungathe kuzisenza tsopano lino. 13Koma atadza Iyeyo, 
              Mzimu wa coonadi, adzatsogolera inu m'coonadi conse; pakuti sadzalankhula 
              za iye mwini; koma zinthu ziri zonse adzazimva, adzazilankhula; 
              ndipo zinthu zirinkudza adzakulalikirani. 14Iyeyo adzalemekeza Ine; 
              cifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu. 15Zinthu ziri 
              zonse Atate ali nazo ndi zanga; cifukwa cace ndinati, kuti atenga 
              za mwa Ine, nadzalalikira kwa inu. Yohane 16: 16-3316Katsala kanthawi, ndipo simundionanso Ine, ndipo kanthawinso, 
              ndipo mudzandiona Ine. 17Mwa akuphunzira ace tsono anati wina ndi 
              mnzace, ici nciani cimene anena ndi ife, Kanthawi ndipo simundiona; 
              ndiponso kanthawi, ndipo mudzandiona; ndipo, cifukwa ndimuka kwa 
              Atate? 18Cifukwa cace ananena, ici nciani cimene anena, Kanthawi? 
              Sitidziwa cimene alankhula.19Yesu anazindikira kuti analikufuna 
              kumfunsa iye, ndipo anati kwa iwo, Kodi mulikufunsana wina ndi mnzace 
              za ici, kuti ndinati, Kanthawi ndipo simundiona Ine, ndiponso kanthawi 
              nimudzandiona Ine? 20Indetu, indetu, ndinena ndi inu, kuti mudzalira 
              ndi kubuma maliro inu, koma dziko lapansi lidzakondwera; mudzacita 
              cisoni inu, koma cisoni canu cidzasandulika cimwemwe. 21Mkazi pamene 
              akuti abale ali naco cisoni, cifukwa yafika nthawi yace; koma pamene 
              wabala mwana, sakumbukilanso kusaukako, cifukwa ca cimwemwe kuti 
              wabadwa munthu ku dziko lapansi. 22Ndipo inu tsono muli naco cisoni 
              tsopano lino, koma ndidzakuonaninso, ndipo mtima wanu udzakondwera, 
              ndipo palibe wina adzacotsa kwa inu cimwemwe canu. 23Ndipo tsiku 
              limenelo simudzandifunsa kanthu. Indetu, indetu, ndinena kwa inu, 
              Ngati mudzapempha Atate kanthu, adzakupatsani inu m'dzina langa. 
              24Kufikira tsopano simunapempha kanthu m'dzina langa; pemphani, 
              ndipo mudzalandira, kuti cimwemwe canu cikwaniridwe.
 25Zinthu izi ndalankhula ndi inu m'mafanizo; ikudza nthawi imene 
              sindidzalankhula ndi inu m'mafanizo, koma ndidzakulalikirani inu 
              momveka za Atate. 26Tsiku limenelo mudzapempha m'dzina langa; ndipo 
              sindinena kwa inu kuti Ine ndidzafunsira inu kwa Atate; 27pakuti 
              Atate yekha akonda inu, cifukwa inu mwandikonda Ine, ndi kukhulupirira 
              kuti Ine ndinaturuka kwa Atate.28Ndinaturuka mwa Atate, ndipo ndadza 
              ku dziko lapansi: ndilisiyanso dziko lapansi, ndipo ndipita kwa 
              Atate.
 29Akuphunzira ace ananena, Onani, tsopano mulankhula zomveka, ndipo 
              mulibe kunena ciphiphiritso, 30Tsopano tidziwa kuti mudziwa zonse, 
              ndipo mulibe kusowa kuti wina akafunse Inu; mwa ici tikhulupirira 
              kuti munaturuka kwa Mulungu. 31Yesu anayankha iwo, Kodi mukhulupirira 
              tsopano? 32Onani ikudza nthawi, ndipo yafika, imene mudzabalalitsidwa, 
              yense ku zace za yekha, ndipo mudzandisiya Ine pa ndekha. Ndipo 
              sindikhala pa ndekha, cifukwa Atate ali pamodzi ndi Ine, 33Zinthu 
              izi ndalankhula ndi inu, kuti mwa Ine mukakhale nao mtendere. M'dziko 
              lapansi mudzakhala naco cibvuto, koma limbikani mtima; ndalilaka 
              dziko lapansi Ine. Mzimu Woyera mu miyoyo yathu 1. a. 1 Yohane 2:2727Ndipo inu, 8 kudzoza kumene munalandira kucokera kwa iye, kukhala 
              mwa inu, ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma 9 monga kudzoza 
              kwace kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli 
              bodza ai, ndipo monga kudaphunzitsa inu, mukhale mwa iye.
  b. Yohane 16: 13-1413Koma atadza Iyeyo, Mzimu wa coonadi, adzatsogolera inu m'coonadi 
              conse; pakuti sadzalankhula za iye mwini; koma zinthu ziri zonse 
              adzazimva, adzazilankhula; ndipo zinthu zirinkudza adzakulalikirani. 
              14Iyeyo adzalemekeza Ine; cifukwa adzatenga za mwa Ine, nadzalalikira 
              kwa inu.
  c. Aroma 8:1414Pakuti onse amene atsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu, amenewo ali 
              ana a Mulungu,
  d. Agalatiya 5: 22-2322Koma cipatso ca Mzimu ndico cikondi, cimwemwe, mtendere, kuleza 
              mtima, cifundo, kukoma mtima, icikhulupirtro, 23cifatso, ciletso; 
              pokana zimenezi palibe lamulo.
  e. Macitidwe 1: 88Komatu mudzalandira mphamvu, Mzimu Woyera atadza pa inu: ndipo 
              mudzakhala mboni zanga m'Yerusalemu, ndi m'Yudeya lonse, ndi m'Samariya, 
              ndi kufikira malekezero ace a dziko.
 Pemphero Marko 1:3535Ndipo m'mawa mwace anauka usikusiku, naturuka namuka kucipululu, 
              napemphera kumeneko.
 2. Macitidwe 8:2626Koma mngelo wa Ambuye analankhula ndi Filipo, nanena, Nyamuka, 
              nupite mbali ya kumwela, kutsata njira yotsika kucokera ku Yerusalemu 
              kunka ku Gaza; ndiyo ya cipululu.
 1 Yohane 5: 14-1514Ndipo uku ndi kulimbika mrima kumene tiri nako kwa iye, kuti ngati 
              tipempha kanthu monga mwa cifuniro cace, atimvera; 15ndipo ngati 
              tidziwa kuti atimvera ciri conse ticipempha, tidziwa kuti tiri nazo 
              izi tazipempha kwa iye.
 3. a. 1 Atesalonika 5:1717Pempherani kosaleka;
  4. a. Mateyu 6: 5-6 5Ndipo pamene mupemphera, musakhale monga onyengawo; cifukwa iwo 
              akonda kuimirira ndi kupemphera m'masunagoge, ndi pa mphambano za 
              makwalala, kuti aonekere kwa anthu. Indetu ndinena kwa inu, Iwo 
              alandiriratu mphotho zao. 6Koma iwe popemphera, Iowa m'cipinda cako, 
              nutseke citseko cako, nupemphere Atate wako ali m'tseri, ndipo Atate 
              wako wakuona m'tseri adzakubwezera iwe.
  b. Masalmo 55:1717Madzulo, m'mawa, ndi msana ndidzadandaula, ndi kubuula, Ndipo 
              adzamva mau anga.
 Kuwerenga Baibulo 1 Akorinto 1:1818Pakuti mau a mtanda ali ndithu cinthu copusa kwa iwo akutayika, 
              koma kwa ife amene tirikupulumutsidwa ali mphamvu ya Mulungu.
 Kumvera  6. Yakobo 1: 22-2522Khalani akucita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha. 
              23Pakuti ngati munthu ali wakumva mau wosati wakucita, iyeyu afanana 
              ndi munthu wakuyang'anira nkhope yace ya cibadwidwe cace m'kalirole; 
              24pakuti wadziyang'anira yekha nacoka, naiwala pompaja nali wotani.25Koma 
              iye wakupenyerera m'lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero cipenyerere, 
              ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakucita nchito, adzakhala 
              wodala m'kucita kwace.
 Agalatiya 5:1717Pakuti thupi lilakalaka potsutsana naye Mzimu, ndi Mzimu potsutsana 
              nalo thupi; pakuti izi sizilingana; kuti zimene muzifuna musazicite.
 1 Akorinto 10:1313Sicinakugwerani inu ciyeso koma ca umunthu; koma Mulungu ali wokhulupirika, 
              amene sadzalola inu kuyesedwa koposa kumene mukhoza; koma pamodzi 
              ndi ciyeso adzaikanso populumukirapo, kuti mudzakhoze kupirirako.
 7. Aefeso 4: 25-3225Mwa ici, mutataya zonama, lankhulani zoona yense ndi mnzace; pakuti 
              tiri ziwalo wina ndi mnzace. 26 Kwiyani, koma musacimwe; dzuwa lisalowe 
              muli cikwiyire, 27ndiponso musampatse malo mdierekezi. 28Wakubayo 
              asabenso; koma makamaka agwiritse nchito, nagwire nchito yokoma 
              ndi manja ace, kuti akhale naco cakucereza wosowa. 29 Nkhani yonse 
              yobvunda isaturuke m'kamwa mwanu, koma ngati pali yina yabwino kukumangirira 
              monga mofunika ndiyo, kuti ipatse cisomo kwa iwo akumva. 30Ndipo 
              musamvetse cisoni Mzimu Woyera wa Mulungu, amene munasindikizidwa 
              cizindikilo mwa iye, kufikira tsiku la maomboledwe. 31 Ciwawo conse, 
              ndi kupsya mtima, ndi mkwiyo, ndi ciwawa, ndi mwano zicotsedwe kwa 
              inu, ndiponso coipa conse.32Koma mukhalirane okoma wina ndi mnzace, 
              a mtima wacifundo,
 1 Akorinto 6: 19-2019Kapena simudziwa kuti thupi lanu liri kacisi wa Mzimu Woyera, 
              amene ali mwa inu, amene muli naye kwa Mulungu? Ndipo simukhala 
              a inu nokha. 20Pakuti munagulidwa ndi mtengo wace wapatali; cifukwa 
              cace lemekezani Mulungu m'thupi lanu.
  8. Agalatiya 5:1616Koma ndinena, Muyendeyende ndi Mzimu, ndipo musafitse cilakolako 
              ca thupi.
   |  |